< 2 Chronicles 32 >

1 After King Hezekiah had obeyed Yahweh’s instructions and had done all those things, King Sennacherib of Assyria came [with his army] and invaded Judah. He commanded his soldiers to surround the cities that had walls around them, thinking that they would [break through those walls and] conquer those cities.
Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
2 When Hezekiah saw that Sennacherib had come [with his army] and that they intended to attack Jerusalem,
Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
3 he consulted with his officials and army leaders. They said among themselves, “Why should we allow the king of Assyria [and his army] to come and find plenty of water to drink?” So they decided to stop the water from flowing outside the city. So a large group of men gathered together and blocked all the springs and the stream that flowed through that area.
iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
4
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
5 Then they worked hard to repair all the sections of the city wall that had been broken, and they built watchtowers on the walls. They built another wall outside/around the wall that was already outside the city, and they strengthened the defenses on the sloping terraces [on the east side of the area called ‘The City of David’]. They also made a large number of weapons and shields.
Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
6 Hezekiah appointed army commanders, and he gathered them in front of him in the square at one of the city gates, and he encouraged them by saying this to them:
Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
7 “Be strong and courageous. Do not be afraid or discouraged on account of the king of Assyria and the huge army that is with him, because [Yahweh] is with us, and his [power] is greater than their [power].
“Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
8 They have to rely on the power of humans, but we have Yahweh our God to help us and to fight battles for us.” So the people became more confident because of what Hezekiah, the king of Judah, said.
Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
9 Later, when Sennacherib and all his soldiers were surrounding Lachish [city], he sent some officers to Jerusalem to give this message to King Hezekiah and to all the people of Judah who were there:
Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
10 “[I am] Sennacherib, the [great] king of Assyria, [and] this is what I say: 'While you are staying in Jerusalem, my soldiers are surrounding the city. So why [RHQ] are you so confident?
“Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
11 Hezekiah says to you, “Yahweh our God will save us from [being defeated by the army of] the king of Assyria,” but he is misleading you. He wants you to die from having no food or water.
Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
12 Isn’t Hezekiah the one who told his men to get rid of your god Yahweh’s shrines and altars on the hilltops, saying to [you people of] Jerusalem and other places in Judah, “You must worship at only one altar and burn sacrifices on only that altar”?
Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
13 'Do you people not know what I and my ancestors have done to all the people-groups in other countries? [We destroyed them all, and] none of the gods of those nations were ever able to prevent my [troops] from conquering them! So how can your god prevent my soldiers from conquering you?
“Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
15 So do not allow Hezekiah to deceive you like this. Do not believe what he says, because no god of any nation or kingdom has ever been able to rescue his people from being conquered by my army and the armies of my ancestors. So certainly your god will not be able to rescue you from my power'.”
Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
16 Sennacherib’s officers said more things to belittle Yahweh the God of the Israelis and Hezekiah, who served God [well].
Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
17 King Sennacherib wrote more letters insulting Yahweh, the God whom the Israelis [belonged to/worshiped]. He said things like this: “The gods [worshiped by] the people-groups in other countries did not rescue their people from my power. Similarly, the god of Hezekiah will not rescue his people from my power.”
Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
18 Then King Sennachereb’s officers shouted in the Hebrew language to the people who were on the wall, in order to cause them to be terrified, thinking that as a result the army of Assyria could capture the city [without a battle].
Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
19 They belittled the God [worshiped by the people] of Jerusalem as they belittled the gods of the other people-groups of the world—saying that they were only [idols] made by humans.
Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
20 Then King Hezekiah and the prophet Isaiah cried out to God, praying about this.
Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
21 And [that night] Yahweh sent an angel who killed all the soldiers of Assyria and their leaders and their officers in the place where the king of Assyria and his army had set up their tents. So the king of Assyria left and returned to his own country, very disgraced. And one day when he went into the temple of his god, some of his sons struck him with their swords and killed him.
Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
22 That is how Yahweh rescued Hezekiah and the people of Jerusalem from the power of Sennacherib, the king of Assyria, and from their other enemies. Yahweh took care of them (OR, gave them peace) everywhere in the country.
Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
23 Many people brought offerings for Yahweh to Jerusalem, and also brought valuable gifts for King Hezekiah. And from that time, Hezekiah was highly respected/honored by the people of all the other nations.
Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
24 About that time, Hezekiah became very ill. He was about to die. But he prayed to Yahweh, and Yahweh answered his prayer. He performed a miracle [and healed Hezekiah].
Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
25 But Hezekiah [SYN] was very proud, and he did not thank Yahweh for being kind to him. Therefore Yahweh was angry with him and [and punished him] and [the people of] Jerusalem and other places in Judah.
Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
26 Then Hezekiah said that he was sorry for being proud, and the people of Jerusalem also said that they were sorry [for their sins]. So Yahweh did not punish them during the remaining years that Hezekiah [was their king].
Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
27 Hezekiah became very rich and was greatly honored. His [workers] made storerooms for his silver and gold, and for his very valuable stones, and for spices and shields and other valuable things.
Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
28 [His workers] also built buildings to store the grain and wine and [olive] oil [that people produced and brought to him]. They also made stalls for various kinds of cattle and pens for his flocks [of sheep and goats].
Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
29 They built towns and acquired for the king many flocks [of sheep and goats] and herds [of cattle], because God had enabled him to become very rich.
Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
30 Hezekiah was the one who told his workers to block the place where the water flows out of the Gihon Spring, and to build a tunnel through which the water flowed to the west side of the area called ‘The City of David’. He was able to do everything that he wanted to do.
Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
31 But when messengers who were sent by the rulers of Babylon came and asked about the miracle that God had performed for him, God allowed Hezekiah to say what he himself wanted to say, in order to test [whether or not Hezekiah would admit that God had performed a miracle].
Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
32 A record of the other things that happened while Hezekiah was ruling, and the things that he did to please God, is on the scroll in which is written the vision that [Yahweh gave to] the prophet Isaiah. It is also written in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah and Israel’.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
33 When Hezekiah died, he was buried in the tombs where the most respected kings [of Judah] were buried. Everyone in Jerusalem and other places in Judah honored him. Then his son Manasseh became the king.
Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 32 >