< 1 Timothy 1 >

1 [I], Paul, [am writing this letter. You know that] I am an apostle. I [represent] Christ Jesus because God and Christ Jesus commanded me to do it. God is the one who saved us, and Jesus is the one for whom we are confidently waiting [to return].
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.
2 [You], Timothy, [are like] [MET] a true son [to me] because [you] trusted [in Christ after I told you about him]. [I pray/desire that] God, who is our Father, and Christ Jesus, who is our Lord, will [continue to act] kindly and mercifully to you, and [that they will give you inner] peace.
Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro. Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.
3 [I urge you now], just like I urged you when I was going to Macedonia [province], that you remain there in Ephesus [city]. Stay there so that you may command certain persons [who teach other believers] that they not teach false [doctrines].
Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga,
4 And tell people to not continually give their attention to stories [that tell about our ancestors], stories in which there are (genealogies/lists of our ancestors’ names) that [seem to be] endless. [You must command your congregation not to think that these stories are valuable], because [whenever people think] that, they [just] start arguing about things uselessly, instead of [teaching] God’s plan, which [is concerned with] what we believe (OR, which [we know because] we trust [in Christ]).
kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro.
5 [Teach them] to have pure desires [MTY] and [so to know that God] approves of what they do, and to sincerely believe [the true teaching]. By doing that, [they will] love [God well].
Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona.
6 There are some people who have turned away from these true teachings. As a result, they [just] discuss what is useless.
Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo.
7 They desire to teach the laws [that God gave to Moses], but they do not understand what they are really saying, or the things about which they (confidently speak/say that they understand well).
Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.
8 We know that the laws [that God gave to Moses are] good if people consider correctly [what God intended them for].
Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino.
9 We must remember that God did not give Moses those laws in order [to condemn] righteous people. By those laws he [condemns people who act as though there were no] laws and who refuse to obey [anyone. He condemns] those who do not revere God and those who sin habitually. [By them he condemns] those who refuse to perform rituals that are pleasing to God and who show no respect for religion. [He condemns] those who murder their fathers and who murder their mothers and who murder [other] people.
Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena.
10 [He condemns] those who are sexually immoral and those who are homosexuals. [He condemns] those who kidnap/steal people [in order to make them slaves]. [He condemns] those who lie and those who promise something strongly but do not do what they promised. He condemns every other action that is contrary to our true teaching.
Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona.
11 This is what we teach people when we tell them the glorious/wonderful message about Christ that our awesome God [has revealed] and that he gave to me to teach.
Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.
12 I am grateful to Christ Jesus our Lord who enabled me to do this work, because he considered that I could be trusted. So he appointed me in order that I [would serve him].
Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake.
13 Formerly I said evil things [about him], I caused [his people] to suffer, and I acted very cruelly toward them. But [Christ acted] in a kind way toward me since I (acted ignorantly/did not know that I was doing wrong) because I did not believe [in him].
Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro.
14 Our Lord kindly did for me what I did not deserve, so that I now believe [in Christ Jesus] and I love others (OR, him) [because I belong to him].
Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.
15 [Something that all we believers] say is certainly true and is worthy for us to fully accept is that Christ Jesus came into the world in order to save sinful people [so that God would not punish them for their sins]. As for me, I [consider that I have sinned] more than all others.
Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa.
16 Yet Christ Jesus acted mercifully to me in order that he might demonstrate [to people that he is perfectly patient with them]. He did that by his being patient with me, one who has sinned worse than everyone else. He wanted what he did for me (to be an example/to demonstrate his patience) to people who would [later] believe in him, and as a result would live forever. (aiōnios g166)
Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. (aiōnios g166)
17 I desire that people will honor and praise the only [true] God forever! Even though no one can see him, he is the King who rules for all time, who will never die! (Amen!/That is true!) (aiōn g165)
Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
18 Timothy, you [are like] [MET] a son [to me]. So, (based on/in accordance with) what [someone] previously (prophesied/told what God revealed to them) about you, I am instructing you [to strongly oppose those who teach false doctrines. You should oppose them like] [MET] a soldier (fights strongly against/opposes) [those who attack his countrymen].
Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo
19 Continue to believe [the true teaching] and do only what you know to be right! Remember that some people have (pushed aside/rejected) the true teaching. As a result, they no longer believe [MET] what is true.
utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka.
20 Among the ones who have done that are Hymenaeus and Alexander, whom I put in the hands of Satan, in order that [when Satan punishes them] they may learn not to teach wrong teaching.
Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.

< 1 Timothy 1 >