< 1 Thessalonians 1 >

1 [I], Paul, [am writing this letter]. Silas and Timothy [are with me]. [We(exc) are sending this letter] to [you who are] the congregation [of believers] in Thessalonica [city]. We [(inc)] all [worship] (OR, [trust in]) God [our] Father [MET] and [our] Lord Jesus Christ. [We three desire/pray that God, our Father, and Jesus Christ, our Lord, will continue to] act kindly toward you and [will continue to] cause you to have [inner] peace.
Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
2 We always thank God for you all [when] we mention you while we pray (OR, [when] we pray [for you]).
Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
3 [We thank God because] we continually remember that you work [for God because] you trust [in him] and you earnestly/energetically help people because you love them. You also endure [it when people cause you to suffer]. You endure it because you confidently expect that our Lord Jesus Christ [will soon return from heaven to rescue you]!
Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 My fellow believers whom God loves, we [also thank him because] we know that he chose you [to become his people].
Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
5 We know that he chose you because [when] we told that message to you, we did not speak only words. The Holy Spirit [helped us to speak] powerfully/effectively, and he strongly assured [us that he was powerfully working in you by means of] the message [about Christ] that we [told to you. You yourselves know that], because you know how we spoke and how we conducted ourselves when we were with you, in order that [we might help] you.
chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
6 We also [know that God chose you] because we have now heard that you have endured your troubles when [people] caused you to suffer very much [because you believed in Christ]. You endured just like the Lord [Jesus Christ] endured, and just like we did [when people caused us to suffer]. At that time you were joyful because the Holy Spirit caused you to be joyful.
Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
7 As a result [of your joyfully enduring your troubles], all the believers who live in Macedonia and Achaia [provinces have heard how firmly you trust God. So they know that they should firmly trust in God] as you do.
Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
8 Other people have heard you tell the message [from] the Lord [Jesus]. Then they also have proclaimed the message to people who live throughout Macedonia and Achaia [provinces]. Not only that, but [people who live] in many far-away places [HYP] have heard that you trust in God. As a result, we do not need to tell people [what God has done in your lives].
Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
9 People [who live far from you are telling others what happened when we were with you]. They also report that you stopped [worshipping things that] ([you/your ancestors]) [considered to be] gods and now you worship God. [As a result], you serve the God who is all-powerful and who is the real God.
pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
10 They tell us that now you wait expectantly for his Son [to return to earth] from heaven. You firmly believe that God caused him to live again after he died. You believe also that Jesus will rescue [all of] us, [who trust in him], from [God’s] punishing us [MTY].
Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.

< 1 Thessalonians 1 >