< 1 Corinthians 6 >

1 [Now another matter]: When any of you [believers] accuses another believer about some matter, he takes that matter to judges who are not believers, [for them to decide the case], instead of asking God’s people [to decide it]. (That is disgusting!/Why do you do that?) [RHQ]
Pamene wina wa inu ali ndi mlandu ndi mnzake, nʼchifukwa chiyani amatengera nkhaniyo kwa anthu akunja kuti akawaweruze mʼmalo mopita nayo kwa oyera mtima?
2 [I want] you to know that [we who are] God’s people will [some day] judge those who are unbelievers. [RHQ] So, since you will be judging unbelievers, you certainly are capable of judging between [believers who disagree on] small matters! [RHQ]
Kodi inu simukudziwa kuti anthu a Mulungu adzaweruza dziko lapansi? Ndipo ngati inu mungaweruze dziko lapansi, kodi sindinu oyenera kuweruza milandu ingʼonoyingʼono?
3 (You should keep in mind that we will even judge angels!/Do you not know that we will even judge angels?) [RHQ] So we certainly should be able to judge about [matters that relate to how we] conduct our lives here on earth!
Kodi simukudziwa kuti mudzaweruza angelo? Nanga bwanji zinthu za mʼmoyo uno!
4 Therefore, when you [believers] have a dispute, you should certainly not choose as judges [to decide your case] people whom the congregation cannot respect [because those judges are not believers]! [RHQ]
Nʼchifukwa chake, ngati pali milandu pa zinthu zotere, sankhani anthu ena kuti akhale oweruza ngakhale alibe udindo mu mpingo.
5 I am saying this to make you ashamed. Surely there is someone among you who is wise enough to judge disputes between believers! [RHQ]
Ndikunena izi kuti ndikuchititseni manyazi. Moti nʼkutheka kuti pakati panu palibe wina wanzeru zokwanira kuti aziweruza mlandu pakati pa Akhristu?
6 But instead, some believers [among you] accuse other believers in a legal court. And what is worse, you let the cases be judged by unbelievers {unbelievers judge the cases}!
Koma mʼmalo mwake mʼbale atengera ku bwalo la mlandu mʼbale mnzake kukaweruzidwa. Zonsezi pamaso pa akunja!
7 The fact that you have any lawsuits among you [shows that] you have completely failed [as Christians] (OR, [allowed Satan to] defeat you). You should [allow other believers] to wrong you [without taking them to court!]! [RHQ] You should not accuse them when [they] cheat you! [RHQ]
Chokha choti mwakasumirana chikuonetseratu kuti mwagonjetsedwa kale. Bwanji osangolola kuti ena akulakwireni? Bwanji osangolola kuti ena akubereni?
8 But [what is happening is that] some of you are cheating others and doing wrong to them. [That is bad]. But you are doing that to fellow believers, [and that is worse]!
Mʼmalo mwake, inuyo ndiye mumabera ena ndi kuwalakwira, ndipo mumachita izi kwa abale anu.
9 (You should keep in mind that wicked people will not become [members of] the group over whom God will rule./Do you not know that wicked people will not become [members of] the group over whom God will rule?) [RHQ] Do not be deceived {Do not deceive yourselves} [by thinking wrongly about these matters]. People who are sexually immoral, or who worship idols, or who (commit adultery/have sex with someone to whom they are not married), or who happily allow others to commit homosexual acts with them, or who take the initiative in committing homosexual acts,
Kodi simukudziwa kuti munthu woyipa sadzalowa mu ufumu wa Mulungu? Musanyengedwe: achigololo, kapena opembedza mafano, kapena achiwerewere, kapena amuna adama, kapena ogonana ndi amuna okhaokha;
10 or who are thieves, or who desire and forcefully seize things that belong to others, or who are drunkards, or who slander others, or who are swindlers, will not enter the place where God rules.
kapena akuba, kapena aumbombo, kapena oledzera, kapena achipongwe, kapena opeza ndalama mwachinyengo sadzalowa mu ufumu wa Mulungu.
11 Some of you previously did things like that. But [God] has freed/cleansed you [MET] [from your sinful behavior]. [He] has set you apart for himself. [He] has erased the record of your sins [because you trusted] [MTY] in the Lord Jesus Christ and because of what the Spirit of our God [has done for you].
Ndipo umu ndi mmene ena mwa inu munalili. Koma munatsukidwa, munayeretsedwa, munalungamitsidwa mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu ndi Mzimu wa Mulungu wathu.
12 [Some of you may say], “God allows us to do anything [that he does not forbid].” But [I would reply], “[That is true], but not everything that God permits us to do helps us.” [Yes, as some of you say], God permits us to do anything [that he does not forbid]. But as for me, I will not let anything make me [its slave; that is, I will not do anything that will gain control over me in such a way that I will not be able to stop doing it].
Inu mumati, “Ine ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Komatu si zonse zimene nʼzothandiza. “Ndili ndi ufulu wochita chilichonse.” Koma sindidzagonjetsedwa ndi chilichonse.
13 [Some of you may also say], “Food is just for [us to put in] the stomach, and the stomach is just for [us to put] food [in]. And since God will do away with food and stomachs [when he gives us our new bodies, what we do with our bodies sexually does not affect us any more than eating food does.” But what you have concluded is wrong, because] the Lord does not [want us to use] our bodies to do sexually immoral things. Instead, the Lord [wants us to use our bodies in ways that please him]. Also, the Lord [wants us to do what is good] for our bodies.
Inu mumati, “Chakudya, kwake nʼkulowa mʼmimba ndipo mimba ntchito yake nʼkulandira chakudyacho.” Koma Mulungu adzawononga zonsezi. Thupi silochitira chigololo, koma la Ambuye, ndipo Ambuye ndiye mwini thupilo.
14 God, by his power, caused the Lord [Jesus] to live again after he died, and he will cause us to live again after we die, [which shows that he is very concerned about our bodies].
Mwamphamvu zake Mulungu anaukitsa Ambuye kwa akufa, ndipo ifenso adzatiukitsa.
15 You should keep in mind that your bodies belong to Christ. [RHQ] So, should I [or any other believer] [RHQ] take our body, which belongs to Christ, and join it [sexually] to a prostitute? No, certainly not!
Kodi simukudziwa kuti matupi anuwo ndi ziwalo za Khristu mwini? Kodi tsono ndingatenge ziwalo za Khristu nʼkuzisandutsa ziwalo za mkazi wadama? Zosatheka!
16 When a man has sexual relations [EUP] with a prostitute, [it is as though] their two bodies become one body. (You should never forget that!/Do you not know that?) [RHQ] What [Moses] wrote [about people who join together sexually is], “The two of them will become [as though they are] one body.”
Kodi simukudziwa kuti amene amadzipereka kwa mkazi wadama, iyeyo ndi mkaziyo amasanduka thupi limodzi? Paja kunalembedwa kuti, “Awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
17 But anyone who is united {who joins himself} to the Lord becomes one with him spiritually.
Koma amene amadzipereka kwa Ambuye, iyeyo ndi Ambuye amakhala mzimu umodzi.
18 Always (run away from/avoid) committing sexually immoral acts. Other sins that people commit do not affect their bodies, but those who commit sexually immoral acts sin against their own bodies.
Thawani dama. Machimo onse amene munthu amachita amakhala kunja kwa thupi lake, koma amene amachita machimo okhudza chigololo, amachimwira thupi lake lomwe.
19 (Keep in mind that your bodies are [like] [MET] temples of the Holy Spirit./Do you not know that your bodies are [like] [MET] temples of the Holy Spirit?) [RHQ] The Spirit, whom God gave you, lives within you. You do not belong to yourselves. You belong to God,
Kodi simukudziwa kuti thupi lanu ndi Nyumba ya Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene mwalandira kuchokera kwa Mulungu? Inu simuli panokha ayi.
20 [because when his Son died for you it was as though] [MET] [God] paid a price for you. So honor God by [how you use] your bodies!
Ndinu ochita kugulidwa. Nʼchifukwa chake lemekezani Mulungu mʼthupi lanu.

< 1 Corinthians 6 >