< 1 Chronicles 23 >

1 David was a very old man [DOU] when he appointed his son Solomon to be the next king.
Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
2 David gathered the leaders of Israel and the priests and other descendants of Levi.
Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
3 He [commanded some of his officials to] count the descendants of Levi who were at least thirty years old, and they found out that there were 38,000 of them.
Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
4 Then David said, “From those 38,000 men, I want 24,000 of them to supervise the work at the temple of Yahweh, and I want 6,000 of them to be officials and judges.
Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
5 I want 4,000 to be guards at the gates, and 4,000 to praise Yahweh, using the musical instruments that I have provided for them.”
Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
6 David divided the descendants of Levi into three family groups; each group consisted of men who were descendants of one of the three sons of Levi—Gershon, Kohath, and Merari.
Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
7 From the descendants of Gershon there were Ladan and Shimei.
Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
8 There were three sons of Ladan: Jehiel was the oldest, and his [younger] brothers Zetham and Joel.
Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
9 There were three of the sons of Shimei: Shelomoth, Haziel, and Haran. They were all leaders of the clans of Ladan.
Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
10 There were four men who were other sons of Shimei:
Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
11 Jahath, who was his oldest son, and his [younger] brothers Ziza, Jeush, and Beriah. Jeush and Beriah did not have many sons, so they were counted as though they were one family.
Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
12 Kohath had four sons: Amram, Izhar, Hebron, and Uzziel.
Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
13 There were two sons of Amram: Aaron and Moses. Aaron and his descendants were set apart to dedicate the very holy things, to offer sacrifices to Yahweh, to serve in his presence, and to declare [to the people] what Yahweh [MTY] would do to bless them. They were to do those things forever.
Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
14 The sons of Moses, the man who served God [well], were counted as part of the tribe of Levi.
Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
15 The sons of Moses were Gershom and Eliezer.
Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
16 The oldest son of Gershom was Shubael.
Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
17 Rehabiah was the oldest son of Eliezer. Eliezer had no other sons, but Rehabiah had many sons.
Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
18 The oldest son of Izhar was Shelomith.
Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
19 Hebron had four sons. Jeriah was his oldest son, and his [younger] brothers were Amariah, Jahaziel, and Jekameam.
Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
20 Uzziel had two sons. Micah was the oldest son, and his [younger] brother was Isshiah.
Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
21 Merari had two sons: Mahli and Mushi. The sons of Mahli were Eleazar and Kish.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
22 Eleazar had no sons; he had only daughters. Their cousins, the sons of Kish, married them.
Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
23 The three sons of Mushi were Mahli, Eder, and Jerimoth.
Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
24 Those were the descendants of Levi, whose names were listed according to their families/clans. They were chosen for special jobs by (casting lots/throwing small marked stones). Each person who was at least 20 years old was listed. They all worked in the temple of Yahweh.
Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
25 David had said previously, “Yahweh, the God to whom we Israeli people belong, has enabled us to have peace, and he [has come to] live in Jerusalem forever.
Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
26 Therefore, the descendants of Levi no longer need to carry the Sacred Tent and the items used in the work there.”
sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
27 Obeying the final instructions of David [before he died, instructions for doing this work at the temple], they counted only the descendants of Levi who were at least 20 years old.
Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
28 The work of those descendants of Levi was to assist the descendants of Aaron in their work in the temple of Yahweh: To be in charge of the temple courtyards and the side rooms, the ceremonies for purifying all the sacred things, and to do other work at the temple.
Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
29 They were also in charge of the sacred loaves of bread that were placed [each week] on the table [in the temple], the flour for the grain offerings, the wafers that were made without yeast, and the measuring the ingredients and mixing them and baking that bread and those wafers.
Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
30 They were also told to stand every morning [at the temple] and thank Yahweh and praise him. They were also required to do the same thing every evening.
Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
31 And they were to do the same thing whenever offerings that were to be completely burned [on the altar] were presented/offered to Yahweh on Sabbath days and during the new moon celebrations and other religious festivals. They were told how many of them should be there and what they should do each time.
ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
32 So the descendants of Levi did the work that was assigned to them by their fellow Israelis who were descendants of Aaron. They did that work in the area surrounding the Sacred Tent, and in the Sacred Tent, and [later] at the temple.
Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.

< 1 Chronicles 23 >