< Hebrews 7 >

1 this/he/she/it for the/this/who Melchizedek king Salem priest the/this/who God the/this/who Highest (the/this/who *N+kO) to meet Abraham to return away from the/this/who slaughter the/this/who king and to praise/bless it/s/he
Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa.
2 which and tenth away from all to divide Abraham first on the other hand to interpret king righteousness then then and king Salem which to be king peace
Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.”
3 fatherless motherless without genealogy neither beginning day neither life goal/tax to have/be to make like then the/this/who son the/this/who God to stay priest toward the/this/who perpetual
Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.
4 to see/experience then how great this/he/she/it which and tenth Abraham to give out from the/this/who fine spoils the/this/who patriarch
Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha.
5 and the/this/who on the other hand out from the/this/who son Levi the/this/who priesthood to take commandment to have/be to tithe the/this/who a people according to the/this/who law this/he/she/it to be the/this/who brother it/s/he although to go out out from the/this/who loins Abraham
Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu.
6 the/this/who then not to trace genealogy out from it/s/he to tithe (the/this/who *k) Abraham and the/this/who to have/be the/this/who promise to praise/bless
Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu.
7 without then all dispute the/this/who lesser by/under: by the/this/who greater to praise/bless
Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo.
8 and here on the other hand tenth to die a human to take there then to testify that/since: that to live
Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo.
9 and as/when a word to say through/because of Abraham and Levi the/this/who tenth to take to tithe
Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu,
10 still for in/on/among the/this/who loins the/this/who father to be when to meet it/s/he (the/this/who *k) Melchizedek
chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.
11 if on the other hand therefore/then perfection through/because of the/this/who Levitical priesthood to be the/this/who a people for upon/to/against (it/s/he to give laws *N+kO) which? still need according to the/this/who order Melchizedek other to arise priest and no according to the/this/who order Aaron to say: call
Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni?
12 to transport for the/this/who priesthood out from necessity and law removal/change to be
Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha.
13 upon/to/against which for to say this/he/she/it tribe other to share away from which none to watch out the/this/who altar
Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe.
14 obvious for that/since: that out from Judah to rise the/this/who lord: God me toward which tribe about (priest *N+KO) none Moses to speak
Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe.
15 and more excessive still evident to be if according to the/this/who likeness Melchizedek to arise priest other
Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki.
16 which no according to law commandment (fleshly *N+kO) to be but according to power life indestructible
Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha.
17 (to testify *N+kO) for that/since: that you priest toward the/this/who an age: eternity according to the/this/who order Melchizedek (aiōn g165)
Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn g165)
18 nullification on the other hand for to be to go/bring before commandment through/because of the/this/who it/s/he weak and useless
Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu.
19 none for to perfect the/this/who law introduction then greater hope through/because of which to come near the/this/who God
Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.
20 and according to just as/how much no without oath
Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro.
21 the/this/who on the other hand for without oath to be priest to be the/this/who then with/after oath through/because of the/this/who to say to/with it/s/he to swear lord: God and no to repent you priest toward the/this/who an age: eternity (according to the/this/who order Melchizedek *K) (aiōn g165)
Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn g165)
22 according to so great (and *no) greater covenant to be guarantor Jesus
Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.
23 and the/this/who on the other hand greater to be to be priest through/because of the/this/who death to prevent to continue
Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi.
24 the/this/who then through/because of the/this/who to stay it/s/he toward the/this/who an age: eternity permanent to have/be the/this/who priesthood (aiōn g165)
Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn g165)
25 whence and to save toward the/this/who completely be able the/this/who to come near/agree through/because of it/s/he the/this/who God always to live toward the/this/who to call on above/for it/s/he
Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.
26 such as this for me (and *no) be proper high-priest sacred innocent pure to separate/leave away from the/this/who sinful and high the/this/who heaven to be
Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku.
27 which no to have/be according to day necessity just as the/this/who high-priest previously above/for the/this/who one's own/private sin sacrifice to carry up then the/this/who the/this/who a people this/he/she/it for to do/make: do once/at once themself to carry up
Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha.
28 the/this/who law for a human to appoint/conduct high-priest to have/be weakness: weak the/this/who word then the/this/who oath the/this/who with/after the/this/who law son toward the/this/who an age: eternity to perfect (aiōn g165)
Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn g165)

< Hebrews 7 >