< Deuteronomy 18 >

1 not to be to/for priest [the] Levi all tribe Levi portion and inheritance with Israel food offering LORD and inheritance his to eat [emph?]
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 and inheritance not to be to/for him in/on/with entrails: among brother: compatriot his LORD he/she/it inheritance his like/as as which to speak: promise to/for him
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 and this to be justice: custom [the] priest from with [the] people from with to sacrifice [the] sacrifice if cattle if sheep and to give: give to/for priest [the] arm and [the] jaw and [the] stomach
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 first: beginning grain your new wine your and oil your and first: beginning fleece flock your to give: give to/for him
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 for in/on/with him to choose LORD God your from all tribe your to/for to stand: stand to/for to minister in/on/with name LORD he/she/it and son: descendant/people his all [the] day
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 and for to come (in): come [the] Levi from one gate: town your from all Israel which he/she/it to sojourn there and to come (in): come in/on/with all desire soul: appetite his to(wards) [the] place which to choose LORD
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 and to minister in/on/with name LORD God his like/as all brother: compatriot his [the] Levi [the] to stand: stand there to/for face: before LORD
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 portion like/as portion to eat to/for alone: besides sale his upon [the] father
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 for you(m. s.) to come (in): come to(wards) [the] land: country/planet which LORD God your to give: give to/for you not to learn: learn to/for to make: do like/as abomination [the] nation [the] they(masc.)
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 not to find in/on/with you to pass son: child his and daughter his in/on/with fire to divine divination to divine and to divine and to practice sorcery
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 and to unite spell and to ask medium and spiritist and to seek to(wards) [the] to die
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 for abomination LORD all to make: do these and in/on/with because of [the] abomination [the] these LORD God your to possess: take [obj] them from face: before your
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 unblemished: blameless to be with LORD God your
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 for [the] nation [the] these which you(m. s.) to possess: take [obj] them to(wards) to divine and to(wards) to divine to hear: hear and you(m. s.) not so to give: allow to/for you LORD God your
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 prophet from entrails: among your from brother: compatriot your like me to arise: establish to/for you LORD God your to(wards) him to hear: hear [emph?]
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 like/as all which to ask from from with LORD God your in/on/with Horeb in/on/with day [the] assembly to/for to say not to add: again to/for to hear: hear [obj] voice LORD God my and [obj] [the] fire [the] great: large [the] this not to see: see still and not to die
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 and to say LORD to(wards) me be good which to speak: speak
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 prophet to arise: establish to/for them from entrails: among brother: compatriot their like you and to give: put word my in/on/with lip his and to speak: speak to(wards) them [obj] all which to command him
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 and to be [the] man which not to hear: hear to(wards) word my which to speak: speak in/on/with name my I to seek from from with him
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 surely [the] prophet which to boil to/for to speak: speak word in/on/with name my [obj] which not to command him to/for to speak: speak and which to speak: speak in/on/with name God another and to die [the] prophet [the] he/she/it
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 and for to say in/on/with heart your how? to know [obj] [the] word which not to speak: speak him LORD
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 which to speak: speak [the] prophet in/on/with name LORD and not to be [the] word and not to come (in): come he/she/it [the] word which not to speak: speak him LORD in/on/with arrogance to speak: speak him [the] prophet not to dread from him
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Deuteronomy 18 >