< 2 Corinthians 8 >

1 to make known then you brother the/this/who grace the/this/who God the/this/who to give in/on/among the/this/who assembly the/this/who Macedonia
Ndipo tsopano, abale, tikufuna kuti mudziwe za chisomo chimene Mulungu wapereka ku mipingo ya ku Makedoniya.
2 that/since: that in/on/among much test pressure the/this/who excess the/this/who joy it/s/he and the/this/who according to depth poverty it/s/he to exceed toward (the/this/who riches *N+kO) the/this/who openness it/s/he
Pakati pa mayesero owawitsa, chimwemwe chawo chosefukira ndi umphawi wawo otheratu, anapereka mowolowamanja kwambiri.
3 that/since: since according to power to testify and (from/with/beside *N+kO) power self-chosen
Motero ndikuchitira umboni kuti anapereka mmene akanathera, ndipo mwinanso kuposera mmene akathera kupereka. Anapereka mosakakamizidwa,
4 with/after much encouragement to pray me the/this/who grace and the/this/who participation the/this/who service the/this/who toward the/this/who holy: saint (to receive me *K)
ndipo anatipempha motiwumiriza kuti tiwapatse mwayi woti nawonso athandize anthu oyera mtima a ku Yudeya.
5 and no as/just as to hope/expect but themself to give first the/this/who lord: God and me through/because of will/desire God
Iwo anachita moposera mmene ife timayembekezera. Choyamba anadzipereka kwa Ambuye ndipo kenaka kwa ife monga mwa chifuniro cha Mulungu.
6 toward the/this/who to plead/comfort me Titus in order that/to as/just as to begin beforehand thus(-ly) and to complete toward you and the/this/who grace this/he/she/it
Choncho tinamupempha Tito kuti atsirize poti nʼkuti atayamba kale ntchito yachisomoyi pakati panu.
7 but just as in/on/among all to exceed faith and word and knowledge and all diligence and the/this/who out from (me *N+KO) in/on/among (you *N+KO) love in order that/to and in/on/among this/he/she/it the/this/who grace to exceed
Popeza pa zinthu zonse munachita bwino, monga pachikhulupiriro, poyankhula, pachidziwitso, pakhama lambiri ndi pachikondi chanu pa ife, onetsetsani kuti muchitenso bwino pachisomo ichi chopereka.
8 no according to command to say but through/because of the/this/who other diligence and the/this/who the/this/who you love genuine to test
Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena.
9 to know for the/this/who grace the/this/who lord: God me Jesus Christ that/since: that through/because of you be poor rich to be in order that/to you the/this/who that poverty be rich
Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.
10 and resolution in/on/among this/he/she/it to give this/he/she/it for you be profitable who/which no alone the/this/who to do/make: do but and the/this/who to will/desire to begin beforehand away from last year
Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka.
11 now then and the/this/who to do/make: do to complete that just as the/this/who eagerness the/this/who to will/desire thus(-ly) and the/this/who to complete out from the/this/who to have/be
Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo.
12 if for the/this/who eagerness to set before insofar as if to have/be (one *k) acceptable no insofar as no to have/be
Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.
13 no for in order that/to another rest you (then *k) pressure
Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana.
14 but out from equality in/on/among the/this/who now time/right time the/this/who you overflow toward the/this/who that deficiency in order that/to and the/this/who that overflow to be toward the/this/who you deficiency that to be equality
Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana,
15 as/just as to write the/this/who the/this/who much no to increase and the/this/who the/this/who little/few no to have little
monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”
16 grace then the/this/who God the/this/who (to give *N+kO) the/this/who it/s/he diligence above/for you in/on/among the/this/who heart Titus
Tithokoze Mulungu amene anayika mu mtima wa Tito changu chomwecho chimene ine ndili nacho pa inu.
17 that/since: since the/this/who on the other hand encouragement to receive eager then be already self-chosen to go out to/with you
Pakuti Tito sanangovomera kokha pempho lathu, koma yekha anafunitsitsa kwambiri kubwera kwa inu mwa iye yekha.
18 to send with then with/after it/s/he the/this/who brother which the/this/who praise in/on/among the/this/who gospel through/because of all the/this/who assembly
Ndipo tikumutumiza pamodzi ndi mʼbale amene mipingo yonse yamuyamikira chifukwa cha utumiki wake wa Uthenga Wabwino.
19 no alone then but and to appoint by/under: by the/this/who assembly companion me (with *NK+o) the/this/who grace this/he/she/it the/this/who to serve by/under: by me to/with the/this/who it/s/he the/this/who lord: God glory and eagerness (me *N+KO)
Chowonjezera china nʼchakuti anasankhidwa ndi mipingo kuti atiperekeze pamene ife tikukapereka zopereka, zimene tikuchita pofuna kupereka ulemu kwa Ambuye mwini ndi kuonetsa kufunitsitsa kwathu pothandiza.
20 to avoid this/he/she/it not one me to criticize in/on/among the/this/who abundance this/he/she/it the/this/who to serve by/under: by me
Tikufuna kupewa kutikayikira kulikonse za mmene tikuyendetsera mphatso zochulukazi.
21 (to care for *N+kO) (for *no) good no alone before lord: God but and before a human
Pakuti tikuyesetsa kuchita zolondola, osati pamaso pa Ambuye pokha komanso pamaso pa anthu.
22 to send with then it/s/he the/this/who brother me which to test in/on/among much often eager to be now then much eager confidence much the/this/who toward you
Kuwonjezera apo, tikuwatumiza pamodzi ndi mʼbale wathu, amene nthawi zambiri watitsimikizira mʼnjira zosiyanasiyana kuti ndi wachangu ndiponso chifukwa ali ndi chikhulupiriro chachikulu mwa inu.
23 whether above/for Titus participant I/we and toward you co-worker whether brother me apostle assembly glory Christ
Kunena za Tito, ndiye mnzanga ndi wogwira naye ntchito pakati panu. Kunena za abale athu, ndiwo oyimirira mipingo ndi olemekezetsa Khristu.
24 the/this/who therefore/then demonstration the/this/who love you and me pride above/for you toward it/s/he (to show *N+kO) (and *k) toward face the/this/who assembly
Choncho anthu amenewa atsimikizireni za chikondi chanu ndipo adziwe chifukwa chimene ife timakunyadirani, kuti mipingo yonse iwone chimenechi.

< 2 Corinthians 8 >