< Matthew 8 >

1 (When was coming down *N+kO) now (He *N+kO) from the mountain followed Him crowds great.
Iye atatsika ku phiri kuja, anthu ambirimbiri anamutsata.
2 And behold a leper (having come near *N+kO) was worshipping Him saying; Lord, if You shall be willing, You are able me to cleanse.
Ndipo munthu wakhate anadza kwa Yesu namugwadira nati, “Ambuye, ngati mufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
3 And having stretched out the hand He touched of him (Jesus *K) saying; I am willing, do be cleansed. And immediately was cleansed his leprosy.
Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” Nthawi yomweyo anachiritsidwa khate lake.
4 And says to him Jesus; do see that to no one may you tell, But do go yourself do show to the priest and do offer the gift that commanded Moses for a testimony to them.
Ndipo Yesu anati kwa iye, “Taona, usawuze wina aliyense. Koma upite kwa mkulu wa ansembe ukadzionetse wekha ndi kupereka mphatso imene Mose analamulira, kuti ukhale umboni kwa iwo.”
5 (When was entering *N+kO) now (He *n+o) (Jesus *k) into Capernaum came to Him a centurion imploring Him
Yesu atalowa mʼKaperenamu, Kenturiyo anabwera kwa Iye napempha chithandizo,
6 and saying; Lord, the servant of mine has been laid in the house paralyzed grievously being tormented.
nati, “Ambuye, wantchito wanga ali chigonere ku nyumba, sakuthanso kuyenda, akumva kuwawa kwambiri.”
7 And He says to him (Jesus: *ko) I myself having come will heal him.
Ndipo Yesu anati kwa iye, “Ine ndibwera kudzamuchiritsa.”
8 And answering (now *o) the centurion was saying; Lord, not I am worthy that my under the roof You may come, but only do speak (a word, *N+kO) and will be healed the servant of mine.
Kenturiyo uja anayankha kuti, “Ambuye, ndine wosayenera kuti Inu mukalowe mʼnyumba mwanga. Koma mungonena mawu ndipo wantchito wanga adzachiritsidwa.
9 Also for I myself a man am under authority (appointed *O) having under myself soldiers and I say to this [one]; do go, and he goes, and to another; do come, and he comes, and to the servant of mine; do enact this, and he enacts [it].
Pakuti inenso ndili pansi pa ulamuliro ndipo ndili ndi asilikali amene ndiwalamulira. Ndikalamulira mmodzi kuti, ‘Pita,’ amapita; ndi kwa wina kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikawuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ iye amachita.”
10 Having heard now Jesus marveled and He said to those following; Amen I say to you; (such *no) (no [one] *N+kO) so great faith in Israel have I found.
Yesu atamva zimenezi, anadabwa ndipo anati kwa omutsatira, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti sindinapeze wina aliyense mu Israeli wachikhulupiriro chachikulu chotere.
11 I say now to you that many from east and west will come and they will recline with Abraham and Isaac and Jacob in the kingdom of the heavens.
Ndikuwuzani kuti ambiri adzabwera kuchokera kummawa ndi kumadzulo, nadzakhala nawo pa phwando pamodzi ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo mu ufumu wakumwamba.
12 the however sons of the kingdom will be cast out into the darkness the outer; there will be the weeping and the gnashing of the teeth.
Koma eni ake ufumuwo adzaponyedwa ku mdima wakunja kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
13 And said Jesus to the centurion; do go, (and *ko) as you have believed it should be [done] to you. And was healed the servant of him in the hour that.
Pamenepo Yesu anati kwa Kenturiyo, “Pita! Zichitike monga momwe wakhulupirira.” Ndipo wantchito wake anachira pa nthawi yomweyo.
14 And having come Jesus to the house of Peter He saw the mother-in-law of him lain down and fevering
Ndipo Yesu atalowa mʼnyumba ya Petro, anaona mpongozi wake wa Petro ali gone akudwala malungo.
15 And He touched the hand of her, and left her the fever. and she arose and was ministering (to him. *N+KO)
Ndipo Yesu anakhudza dzanja lake ndipo pomwepo anachira nayamba kumutumikira.
16 When evening now having come they brought to Him being demonised many, and He cast out the spirits by a word, and all those sick being He healed,
Itafika nthawi yamadzulo, anthu anabweretsa kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi ziwanda ndipo anatulutsa ziwandazo ndi mawu okha, nachiritsa odwala onse.
17 so that it may be fulfilled that having been spoken through Isaiah the prophet saying; Himself the infirmities of us He took and [our] diseases bore.
Uku kunali kukwaniritsa zimene ananena mneneri Yesaya kuti, “Iye anatenga zofowoka zathu, nanyamula nthenda zathu.”
18 Having seen now Jesus (great *KO) (crowd *N+kO) around Him He commanded to depart to the other side.
Yesu ataona gulu la anthu litamuzungulira, analamula kuti awolokere kutsidya lina la nyanja.
19 And having come to [Him] one scribe said to Him; Teacher, I will follow You wherever if You shall go.
Ndipo mphunzitsi wa malamulo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ine ndidzakutsatani kulikonse kumene muzipita.”
20 And says to him Jesus; Foxes holes have and the birds of the air nests, but the Son of Man no has [place] where the head He may lay.
Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ndi mbalame zamlengalenga zili ndi zisa, koma Mwana wa Munthu alibe malo ogona ngakhale potsamira mutu wake.”
21 Another now of the disciples of Him said to Him; Lord, do allow me first to go and to bury the father of mine.
Wophunzira wina anati kwa Iye, “Ambuye, mundilole ndiyambe ndakayika maliro a abambo anga.”
22 But Jesus (speaks *N+kO) to him; do follow Me, and do leave the dead to bury their own dead.
Koma Yesu anamuwuza kuti, “Nditsate Ine ndipo uwaleke akufa ayikane akufa okhaokha.”
23 And having climbed He into the boat followed Him the disciples of Him.
Iye atalowa mʼbwato, ophunzira ake anamutsatira.
24 And behold a storm great arose in the sea so that the boat being swamped by the waves; He Himself however was sleeping.
Ndipo taonani mwadzidzidzi mphepo yayikulu yamkuntho inawomba pa nyanjapo, kotero kuti bwatolo linayamba kumizidwa ndi mafunde. Koma Yesu anali mtulo.
25 And having come to [Him] (the disciples of Him *k) they awoke Him saying; Lord, do save (us *k) we are perishing!
Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”
26 And He says to them; Why fearful are you, O [you] of little faith? Then having arisen He rebuked the winds and the sea, and there was a calm great.
Iye anawayankha kuti, “Inu achikhulupiriro chochepa, chifukwa chiyani mukuchita mantha?” Ndipo anayimirira nadzudzula mphepoyo ndi mafunde ndipo panali bata lalikulu.
27 And the men marveled saying; What kind [of man] is this that even the winds and the sea Him obey
Ndipo ophunzirawo anadabwa nafunsa kuti, “Ndi munthu wotani uyu? Kuti ngakhale mphepo ndi mafunde zimvera Iye!”
28 And (when was coming He *N+kO) to the other side to the region of the (Gadarenes *N+KO) met Him two being demonised out of the tombs coming forth, violent extremely, so that not to be able anyone to pass through the way that.
Ndipo atafika ku mbali ina ya dera la Gadara, anakumana ndi anthu awiri ogwidwa ndi ziwanda akuchokera ku manda. Iwowa anali woopsa kwambiri kotero kuti panalibe munthu akanatha kudzera njira imeneyo.
29 And behold they cried out saying; What to us and to you (Jesus *k) Son of God? Are You come here before [the] time to torment us?
Ndipo iwo anafuwulira kwa Yesu nati, “Mukufuna chiyani kwa ife, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthawi yake isanafike?”
30 There was now far off from them a herd of pigs many feeding.
Ndipo patali pake panali gulu la nkhumba zimene zimadya.
31 And the demons were begging Him saying; If You cast out us, (do allow *K) (do send away *N+KO) (us *N+kO) into the herd of pigs.
Ndipo ziwandazo zinamupempha Yesu kuti, “Ngati mutitulutsa ife mutitumize mu nkhumba izo.”
32 And He said to them; do go. And having gone out they went away into (herd *k) (pigs, *N+kO) and behold rushed all the herd (of the of pigs *k) down the steep bank into the sea, and perished in the waters.
Iye anati kwa ziwandazo, “Pitani!” Ndipo pamenepo zinatuluka ndi kukalowa mʼnkhumbazo ndipo nkhumba zonse zinathamangira mʼnyanja ndi kufera momwemo.
33 Those now feeding [them] fled, and having gone away into the city they related everything including the [matter] of those being demonised.
Koma amene amaziweta anathawa nalowa mʼmudzi nafotokoza zonse, kuphatikizapo zimene zinachitika ndi anthu ogwidwa ndi ziwanda aja.
34 And behold all the city went out to (meet *N+kO) Jesus, And having seen Him they begged [Him] that He may depart from the region of them.
Ndipo anthu onse a mʼmudziwo anatuluka kukakumana ndi Yesu. Ndipo atamuona Iye, anamupempha kuti achoke mʼdera lawo.

< Matthew 8 >