< Job 8 >

1 And he answered Bildad the Shuhite and he said.
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Until when? will you say these [things] and [will be] a wind mighty [the] words of mouth your.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 ¿ God does he pervert justice and or? [the] Almighty does he pervert righteousness.
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 If children your they sinned to him and he sent them in [the] hand of transgression their.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 If you you will seek God and to [the] Almighty you will seek favor.
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 If [are] pure and upright you for now he will awake on you and he will restore [the] abode of righteousness your.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 And it will be beginning your a small thing and future your it will grow exceedingly.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 For ask please of a generation former and give attention to [the] searching of ancestors their.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 For [are] yesterday we and not we know that [are] a shadow days our on earth.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 ¿ Not they will they instruct you will they say? to you and from heart their will they bring forth? words.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 ¿ Will it grow tall papyrus with not marsh will it grow? reed[s] not water.
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Still it [is] in greenness its not it is plucked off and before any herbage it is dried up.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 [are] thus [the] paths of All [those who] forget God and [the] hope of [the] godless it will be lost.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 [the one] who It snaps confidence his and [is the] house of a spider trust his.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He supports himself on house his and not it stands he takes hold on it and not it endures.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 [is] a fresh [plant] He before [the] sun and over garden its young shoot[s] its it goes out.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Over a heap roots its they are interwoven between stones it sees.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 If someone will swallow it from place its and it will deny it not I have seen you.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 There! that [is] [the] joy of way its and from [the] dust another they will spring up.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 There! God not he rejects a blameless [person] and not he takes hold on [the] hand of evil-doers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Until he will fill laughter mouth your and lips your a shout of joy.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 [those who] hate You they will be clothed shame and [the] tent of wicked [people] there not [will be] it.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >