< Hebrews 10 >

1 A shadow for having the law of the coming good things, not themselves the form of the things, each year with the same sacrifices which they offer to the continuous never (is able *NK+o) those drawing near to perfect;
Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza.
2 Otherwise not would they have ceased being offered because of none having any longer conscience of sins those serving once (cleansed! *N+KO)
Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo.
3 But in these [there is] a reminder of sins every year;
Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka.
4 Impossible [it is] indeed [for the] blood of bulls and of goats to take away sins.
Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.
5 Therefore coming into the world He says: Sacrifice and offering not You have desired, a body however You have prepared me;
Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati, “Simunafune nsembe kapena zopereka, koma thupi munandikonzera.
6 Burnt offerings and [offerings] for sin not You have delighted in;
Simunakondwere nazo nsembe zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.
7 Then I said; Behold I have come — in [the] scroll of [the] book it has been written of Me — to do, O God, the will of You.
Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine, Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’”
8 Above saying that (sacrifices *N+KO) and (offerings *N+KO) and burnt offerings and [offerings] for sin not You have desired nor You delighted in, which according to (the *k) Law are offered,
Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe.
9 then He has said; Behold I have come to do (of the God *K) the will of You. He takes away the first that the second He may establish;
Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri.
10 By that will sanctified we are through the offering of the body of Jesus Christ once for all.
Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.
11 And every indeed priest has stood every day ministering and the same repeatedly offering sacrifices, which never are able to take away sins;
Wansembe aliyense amayimirira tsiku ndi tsiku nʼkutumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza, nsembe zimene sizingathe kuchotsa machimo.
12 (This [One] *N+kO) however one for sins having offered sacrifice in perpetuity sat down at [the] right hand of God,
Koma pamene wansembe uyu anapereka kamodzi kokha nsembe imodzi yokha chifukwa cha machimo, Iye anakhala pansi ku dzanja lamanja la Mulungu.
13 the henceforth awaiting until may be placed the enemies of Him [as] a footstool for the feet of Him.
Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu asandutse adani ake kukhala chopondapo mapazi ake.
14 By one for offering He has perfected for all time those being sanctified.
Chifukwa cha nsembe imodzi Iye anasandutsa angwiro kwamuyaya iwo amene akuwayeretsa.
15 Bears witness now to us also the Spirit Holy; after for (to have said: *N+KO)
Mzimu Woyera nayenso akuchitira umboni za zimenezi kwa ife. Poyamba Iye anati,
16 This [is] the covenant that I will make with them after the days those, says [the] Lord, putting [the] laws of Mine into [the] hearts of them and into (the mind *N+kO) of them I will inscribe them;
“Ili ndi pangano limene ndidzachita nawo atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika malamulo anga mʼmitima mwawo, ndipo ndidzawalemba mʼmaganizo mwawo.”
17 and The sins of them and the lawless acts of them certainly not (will I remember *N+kO) any more.
Ndipo akutinso: “Sindidzakumbukiranso konse machimo awo ndi zolakwa zawo.”
18 Where now forgiveness of these [is], no longer no longer an offering for sin.
Ndipo pamene machimo akhululukidwa, sipafunikanso nsembe yoperekedwa chifukwa cha machimowo.
19 Having therefore, brothers, confidence for the entering to the Holy [Places] by the blood of Jesus,
Ndipo tsono abale, molimba mtima timalowa mʼMalo Opatulika kwambiri chifukwa cha magazi a Yesu.
20 which He dedicated for us a way new and living through the veil, That is through the flesh of Him,
Iye anatitsekulira njira yatsopano ndi yamoyo kudutsa chinsalu chotchinga, chimene ndi thupi lake.
21 and [having] a priest great over the house of God,
Ndiponso tili ndi wansembe wamkulu woyangʼanira nyumba ya Mulungu.
22 we may draw near with a sincere heart in full assurance of faith sprinkled clean [our] hearts from a conscience evil and (having ourselves washed *N+kO) [our] body with water pure.
Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera.
23 We may hold fast to the confession of [our] hope firmly, faithful for [is] the [One] having promised,
Tiyeni tigwiritsitse mosagwedezeka zimene timaziyembekezera ndi kuzivomereza, pakuti amene anatilonjezayo ndi wokhulupirika.
24 And we may think one another toward stirring up to love and to good works
Tiziganizira mmene tingalimbikitsirane wina ndi mnzake pokondana ndi kuchita ntchito zabwino.
25 not forsaking the assembling together of ourselves even as [is the] custom with some, but encouraging [one another], and so much more as much as you see drawing near the Day.
Tiyeni tisaleke kusonkhana kwathu pamodzi monga mmene ena amachitira, koma tizilimbikitsana makamaka poona kuti tsiku la Ambuye layandikira.
26 [If] willingly for sin we after [we are] to receive the knowledge of the truth no longer no longer for sins remains a sacrifice,
Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.
27 terrifying however a certain expectation of judgment and of fire fury to devour being about the adversaries.
Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu
28 Having set aside anyone [the] law of Moses without mercies on the basis of two or three witnesses he dies;
Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu.
29 How much think you worse will he deserve punishment the [one] the Son of God having trampled upon and the blood of the covenant ordinary having esteemed by which he was sanctified and the Spirit of grace having insulted?
Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo?
30 We know for the [One] having said; Mine [is] vengeance, I myself will repay (says Lord; *K) and again: Will judge [the] Lord the people of Him.
Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”
31 [It is] a fearful thing to fall into [the] hands of God [the] living.
Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.
32 do remember however the former days in which having been enlightened a great conflict you endured of sufferings,
Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri.
33 this indeed by revilings both and by tribulations being made a spectacle, this however partners of those thus passing through [them] having become;
Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere.
34 Both for with the (prisoners *N+KO) you sympathized and the plundering of the possessions of you with joy you accepted knowing to have (in *k) (yourselves *N+kO) (a better *NK+o) possession (in heavens *K) and abiding.
Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.
35 Not may throw away therefore the boldness of you, which has a great reward.
Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu.
36 Of endurance for You have need, so that the will of God having done you may receive the promise.
Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza.
37 Yet for A little very while, the [One] who is coming will come and not will delay.
Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe, Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.
38 The one however righteous (of Mine *NO) by faith will live; and if he shall shrink back, not takes pleasure the soul of Mine in him.
Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro. Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha, Ine sindidzakondwera naye.
39 We ourselves however not are of [those] drawing back to destruction but of faith to [the] preserving [of the] soul.
Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.

< Hebrews 10 >