< 2 Corinthians 2 >

1 I judged (for *N+kO) within myself this not again in grief to you to come.
Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko.
2 If for I myself grieve you again who (is *k) the [one] gladdening me except not the [one] being grieved by me?
Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni?
3 And I wrote (to you *k) this same thing, so that not having come grief (I may have *N+kO) from [those] of whom it was necessary me to rejoice having trusted in all you that my joy of all of you is.
Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe.
4 Out of for much affliction and anguish of heart I wrote to you through many tears, not that you may be grieved, but the love that you may know that I have more abundantly toward you.
Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.
5 If however anyone has caused grief, not me myself has he grieved but in part — that not I may burden all you.
Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera.
6 Sufficient to such a one [is] the punishment this which [is] by the majority,
Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira.
7 so that on the contrary rather for you to forgive and to comfort [him], lest perhaps by more excessive sorrow may be overwhelmed such a one.
Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima.
8 Therefore I exhort you to confirm toward him love.
Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye.
9 For this indeed also did I write, so that I may know the proof of you, whether to everything obedient you are.
Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse.
10 To whomever now anything you forgive, I also myself; I also myself; and for I myself (to whom *N+kO) I have forgiven, if anything I have forgiven, [it is] for you in [the] presence of Christ,
Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu,
11 so that not we may be outwitted by Satan; not for of his schemes we are ignorant.
kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.
12 Having come now to Troas for the gospel of Christ also a door to me having been opened in [the] Lord,
Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo,
13 not I have had rest in the spirit of mine in the not finding my Titus the brother of mine, instead having taken leave of them I went out to Macedonia.
ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.
14 However to God [be] thanks to the [One] always leading in triumph us in Christ and the fragrance of the knowledge of Him making manifest through us in every place,
Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino.
15 For of Christ a sweet perfume we are to God in those being saved and in those perishing,
Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka.
16 to one indeed an odor (from *no) death to death, to one however a fragrance (from *no) life to life. And for these things who [is] sufficient?
Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi?
17 Not for we are like the (many *NK+O) peddling the word of God, but as of sincerity, but as of God, (before *N+kO) God in Christ we speak.
Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.

< 2 Corinthians 2 >