< Psalms 30 >

1 A Melody. A Song for the Dedication of the House. David’s. I will extol thee, O Yahweh, for thou hast drawn me up, —and not suffered my foes to rejoice over me.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
2 O Yahweh, my God, I cried for help unto thee, and thou hast healed me.
Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
3 O Yahweh! thou hast lifted, out of hades, my soul, Thou hast brought me back to life, from among those who were going down to the pit. (Sheol h7585)
Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
4 Sweep the strings to Yahweh, ye his men of lovingkindness, and give ye praise at the mention of his holiness.
Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
5 For there is, a Moment, in his anger, a Life-time, in his good-pleasure, In the evening, cometh Weeping to lodge, But, by the morning,’tis a Shout of Triumph!
Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
6 But, I, said, in my tranquility, I shall not be shaken to times age-abiding!
Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
7 O Yahweh, in thy good-pleasure, hadst thou caused my mountain to stand, strong, —Thou didst hide thy face—I was dismayed!
Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
8 Unto thee, O Yahweh, do I cry, —and, unto My Lord, do I make supplication:
Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
9 What profit in my blood? in my going down into the pit? Can dust praise thee? Can it declare thy faithfulness?
“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
10 Hear, O Yahweh, and show me favour, O Yahweh! become thou a helper unto me.
Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
11 Thou hast turned my lamentation, into a dance for me, —Thou hast torn off my sackcloth, and girded me with gladness:
Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
12 To the end that mine honour should make melody unto thee, and not be silent. O Yahweh, my God! Unto times age-abiding, will I praise thee.
kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

< Psalms 30 >