< Psalms 17 >

1 A Prayer of David. Hear, O Yahweh, the right, Attend to my loud cry, Give ear unto my prayer, on lips that would not deceive:
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 From before thee, let my sentence come forth, Thine eyes, behold with equity.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Thou hast tested my heart, hast made inspection by night, hast refined me until thou couldst find nothing, Had I devised evil, my mouth should not have transgressed:
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 As for the workings of men, By the word of thy lips, have, I, taken heed of the paths of the violent one.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Thou hast held fast my goings on to thy ways, My footsteps have not been shaken:
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 I, have called upon thee, for thou wilt answer me, O GOD, —Incline thine ear unto me, Hear thou my speech:
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Let thy lovingkindness be distinguished, thou Saviour of such as seek refuge from them who lift themselves up against thy right hand.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Guard me, as the pupil of the eye, —Under the shadow of thy wings, wilt thou hide me:
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 From the face of lawless ones who have treated me with violence, the foes of my soul, who come round against me:
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Their own fat [heart], have they shut up, —With their mouth, have they spoken proudly.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 As for our own goings, now, have they surrounded us, —Their eyes, they fix, bending to the earth:
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 His likeness, is as a lion, that longeth to rend, and as a young lion, lurking in secret places.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Rise, Yahweh! Confront his face, Bring him down, Deliver my soul from the lawless one [who is] thy sword:
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 From men [who are] thy hand, O Yahweh, From the men of this age, whose portion, is among the living, and, with thy treasure, thou fillest their bosom, —They must be satisfied with sons, And must leave their abundance to their children: —
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 I, in righteousness, shall behold thy face, Shall be satisfied when awakened by a vision of thee.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

< Psalms 17 >