< Psalms 146 >

1 Praise ye Yah, Praise, O my soul, Yahweh.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 I will praise Yahweh while I live! I will make melody to my God while I continue!
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Do not ye trust in nobles, in a son of man who hath no deliverance:
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 His spirit, goeth forth, he returneth to his ground, In that very day, his thoughts perish.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 How happy is he that hath the GOD of Jacob as his help, whose hope, is on Yahweh his God: —
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 Who made The heavens and the earth, The sea and all that is therein, Who keepeth faithfulness to times age-abiding:
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 Who executeth justice for the oppressed, who giveth food to the famishing, Yahweh, who liberateth prisoners;
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 Yahweh, who opened [the eyes of] the blind, Yahweh, who raiseth the prostrate, Yahweh, who loveth the righteous;
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Yahweh, who preserveth sojourners, The fatherless and widows, he relieveth, —but, the way of the lawless, he overturneth.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Yahweh, will reign, to times age-abiding, Thy God, O Zion, to generation after generation. Praise ye Yah!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Psalms 146 >