< Psalms 125 >

1 A Song of Ascents. They who trust in Yahweh, [are] like Mount Zion, which shall not be shaken, Age-abidingly, shall it remain.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Jerusalem! mountains, are round about her; and Yahweh, is round about his people, from henceforth even unto times age-abiding.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 For the sceptre of lawlessness shall not remain over the allotment of the righteous, —lest the righteous put forth—unto perversity—their hands.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Do good, O Yahweh, unto such as are good, even unto such as are upright in their hearts.
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 As for them who turn aside unto their crooked ways, Yahweh, will lead them forth, with the workers of iniquity, Prosperity on Israel!
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.

< Psalms 125 >