< Psalms 124 >

1 A Song of Ascents. David’s. If it had not been, Yahweh, who was on our side, oh might Israel say:
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
2 If it had not been, Yahweh, who was on our side, when men rose up against us,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
3 Then, alive, had they swallowed us up, in the glow of their anger against us;
iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
4 Then, the waters, had whelmed us, the torrent, gone over our soul;
chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
5 Then, had gone over our soul the waters so proud!
madzi a mkokomo akanatikokolola.
6 Blessed, be Yahweh, who gave us not as prey to their teeth.
Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Our soul, as a bird, hath escaped from the snare of the fowlers, The snare, is broken, and, we, are escaped:
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
8 Our help, is in the Name of Yahweh, who made heaven and earth.
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

< Psalms 124 >