< Psalms 114 >

1 When Israel came forth out of Egypt, The house of Jacob from among a people of strange tongue,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Judah became his sanctuary, Israel his realm:
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 The sea, beheld, and fled, The Jordan, turned back;
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 The mountains, started like rams, The hills like the young of the flock?
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 What aileth thee, O sea, that thou fleest? O Jordan, that thou turnest back?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Ye mountains, that ye start like rams? Ye hills, like the young of the flock?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Before the Lord, be in anguish, O earth, Before the GOD of Jacob:
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Who turneth The Rock into a pool of water, The Flint into springs of water.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalms 114 >