< Psalms 108 >

1 A Song, a Melody: David’s. Fixed, is my heart, O God, I will sing and touch the strings, even mine honour.
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 Awake, O harp and lyre, I will awaken the dawn!
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 I will thank thee among the peoples, O Yahweh, and will sing praise unto thee, among the tribes of men.
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 For, great, above the heavens, is thy lovingkindness, and, as far as the skies, thy faithfulness.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Be thou exalted above the heavens, O God, And, above all the earth, be thy glory.
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 To the end thy beloved ones may be delivered, Oh save thou with thy right hand and answer me!
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 God, hath spoken in his holiness, I will exult! I will apportion Shechem! And, the Vale of Succoth, will I measure out;
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 Mine, is Gilead—mine, Manasseh, but, Ephraim, is the defence of my head, Judah, is my commander’s staff;
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 Moab, is my wash-bowl, Upon Edom, will I throw my shoe, Over Philistia, raise a shout of triumph.
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 Who will conduct me to a fortified city? Who will lead me as far as Edom?
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Hast not thou, O God, rejected us? and wilt not go forth, O God, with our hosts.
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 Grant us help out of distress, for, vain, is the deliverance of man:
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 In God, shall we do valiantly, He himself, therefore, shall tread down our adversaries.
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< Psalms 108 >