< Psalms 102 >

1 A Prayer for the Humbled One when he is about to faint, and, before Yahweh, poureth out his grief. O Yahweh, hear thou my prayer, and let, my cry for help, unto thee, enter in.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Do not hide thy face from me, In the day when I am in distress, —Bend down unto me thine ear, In the day when I call, speedily answer me.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 For, consumed in smoke, are my days, And, my bones, like a burning mass, are scorched through;
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Smitten like herbage, so is my heart dried up, For I have forgotten to eat my food.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 At the noise of my groaning, my bone, hath cleaved, to my flesh:
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 I am like the pelican of the desert, I have become as an owl among ruins.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 I have watched and am become, Like a bird sitting alone upon a housetop.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 All the day, have mine enemies, reproached me, And, they who are mad against me, by me, have sworn.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 For, ashes—like bread, have I eaten, And, my drink—with my tears, have I mingled;
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 Because of thine indignation and thy wrath, For thou hast lifted me up, and cast me down.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 My days, are like a shadow extended, And, I, as green herbage, do wither.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 But, thou, O Yahweh, age-abidingly wilt remain, And the memorial of thee, to generation after generation.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Thou, wilt arise, wilt have compassion upon Zion, Surely it is time to favour her, Surely the time appointed, hath come;
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Seeing that thy servants, take pleasure, in her stones, And, her dust, they favour:
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 That the nations may revere thy Name, O Yahweh, And all the kings of the earth, thy glory.
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 When Yahweh, hath built up, Zion, Hath appeared in his glory;
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Hath turned towards the prayer of the destitute, And not despised their prayer,
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 This, shall be written, for a later generation, And, a people to be created, will give praise unto Yah: —
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 That he looked down, out of his holy height, Yahweh, from the heavens unto the earth, directed his gaze; —
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 To hear the groaning of the prisoner, To set free, them who were appointed to death.
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 To the end the Name of Yahweh, might be celebrated in Zion, And his praise in Jerusalem:
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 When the peoples, gather themselves together, And the kingdoms, to serve Yahweh.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 He hath prostrated, in the way, my strength, —He hath shortened my days.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 I said, O my GOD, do not remove me in the midst of my days, Throughout the generation of generations, are thy years;
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Of old—the earth, thou didst found, And, the work of thy hands, are the heavens;
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 They, shall perish, But, thou, wilt abide; And, they all, like a garment, shall fall in pieces, As a vesture, wilt thou change them and they shall vanish;
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 But, thou, art, the same, —And, thy years, shall have no end:
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 The children of thy servants, shall continue, —And, their seed, before thee, be established.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Psalms 102 >