< Proverbs 3 >

1 My son, mine instruction, do not thou forget, and, my commandment, let thy heart observe;
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 For, length of days and years of life, and blessedness, shall they add to thee.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Lovingkindness and faithfulness, let them not forsake thee, —bind them, upon thy neck, write them upon the tablet of thy heart:
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 So find thou favour and good repute, in the eyes of God and man.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Trust thou in Yahweh, with all thy heart, and, unto thine own understanding, do not lean:
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 In all thy ways, acknowledge him, and, he, will make straight thy paths.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Do not become wise in thine own eyes, revere Yahweh, and avoid evil:
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Healing, shall it be to thy body, and refreshing, to thy bones.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honour thou Yahweh, with thy substance, and with the firstfruit of all thine increase;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 So shall thy storehouses be filled with plenty, and, with new wine, shall thy vats overflow.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 The, chastening of Yahweh, my son, do not reject, nor loathe his rebuke;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 For, whom Yahweh loveth, he correcteth, he causeth pain to the son in whom he delighteth.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 How happy the man who hath found wisdom, and the man who draweth forth understanding,
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 For better is her merchandise, than the merchandise of silver, yea, than gold, her increase;
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 More precious, is she, than corals, yea, none of thy delightful things, doth equal her:
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Length of days, is in her right hand, in her left, are riches and honour;
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Her ways, are ways of pleasantness, and, all her paths, are peace;
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 A tree of life, is she, to them who secure her, —and, they who hold her fast, are every one to be pronounced happy.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Yahweh, in wisdom, founded the earth, establishing the heavens with understanding;
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 By his knowledge, the resounding deeps were burst open, and, the skies, drop down dew.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 My son, let them not depart from thine eyes, guard thou counsel, and purpose:
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 So shall they become life to thy soul, and an adorning to thy neck;
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Then, shalt thou walk securely in thy way, and, thy foot, shall not stumble;
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 When thou sittest down, thou shalt have no dread, yea thou shalt lie down, and sweet shall be thy sleep.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Be not thou afraid of sudden dread, nor of the desolation of the lawless, when it cometh.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 For, Yahweh, will be in all thy ways, and will keep thy foot from the snare.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Withhold not good from them who ask it, when it is in power of thy hand to do it:
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Do not say to thy neighbour, Go and come again, and to-morrow I will give, when thou hast it by thee.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Devise not against thy neighbour an injury, seeing that, he, dwelleth securely by thee.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Contend not with a man without cause, if he hath dealt thee no wrong.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Do not thou envy the man of violence, neither choose thou any of his ways;
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 For, an abomination to Yahweh, is the tortuous man, but, with the upright, he is intimate.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 The curse of Yahweh, is in the house of the lawless one, but, the home of the righteous, he blesseth.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Though at scoffers he scoffeth, yet, to the humbled, he granteth favour.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Honour, shall the wise inherit, —but, as for dullards, shame shall carry them away.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbs 3 >