< Numbers 31 >

1 Then spake Yahweh unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Exact thou the avenging of the sons of Israel, from the Midianites, —and, afterwards, shalt thou be withdrawn unto thy kinsfolk.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 So Moses spake unto the people saying, Arm ye from among you men, for the war, and let them go against Midian, to render the avenging of Yahweh upon Midian.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 A thousand from each tribe, —of all the tribes of Israel, shall ye send forth unto the war.
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 And there volunteered out of the thousands of Israel, a thousand of each tribe, —twelve thousand, armed for war.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 And Moses sent them a thousand of each tribe to the war, —them, and Phinehas son of Eleazar the priest, to the war, with the vessels of the sanctuary, and the alarm trumpets, in his hand.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 So they made war upon Midian, as Yahweh had commanded Moses, and slew every male:
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 and the kings of Midian, slew they besides their other slain namely, Evi, and Rekem, and Zur, and Hur, and Reba, five kings of Midian, —Balaam also, son of Beor, slew they with the sword.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 And the sons of Israel took captive the women of Midian and their little ones, —all their cattle also and all their flocks and all their substance, carried they off as a prey;
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 all their cities also in their sites, and all their encampments, burned they up with fire.
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 Then took they all the spoil, and all the booty, —both of man and beast;
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 and brought in unto Moses and unto Eleazar the priest and unto the assembly of the sons of Israel—the captives and the booty, and the spoil unto the camp, —unto the waste plains of Moab, which are by Jordan, near Jericho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 And Moses, and Eleazar the priest and all the princes of the assembly, went forth to meet them, —unto the outside of the camp.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 Then was Moses sore displeased with the officers of the force, —the princes of thousands, and the princes of hundreds who were coming in from the warring host.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 And Moses said unto them, —Have ye saved alive every female?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Lo! they, became unto the sons of Israel, by the advice of Balaam, the cause of daring acts of treachery against Yahweh, over the affair of Peor, —and then came the plague against the assembly of Yahweh!
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Now, therefore, slay ye every male among the young, —every woman also that hath cohabited with man, slay ye.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 But all the young of womankind that have, not cohabited with man, preserve alive for yourselves.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 Ye, then, pitch outside the camp, for seven days, —whosoever hath killed a person and whoever hath touched the slain, cleanse yourselves (from sin) on the third day and on the seventh day ye and your captives,
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Every garment also, and every article of skin and every thing made of goat’s-hair, and every article of wood, shall ye cleanse (from sin).
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 Then said Eleazar the priest unto the men of the host, who had been to the war: This, is the statute of the law, which Yahweh hath commanded Moses:
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 Surely the gold and the silver, —the bronze the iron, the tin and the lead,
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 whatsoever thing can go into fire, ye shall pass through fire and it shall be clean, only with the water of separation, shall ye cleanse it (from sin). But whatsoever cannot go into fire, ye shall pass through water.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 And ye shall wash your clothes on the seventh day, and be clean, —and after-wards, shall ye come into the camp.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 Then spake Yahweh unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Reckon thou up the sum of the booty that was captured, both of man and of beast, —thou and Eleazar the priest, and the ancestral heads of the assembly;
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 and divide the booty into two parts, between them who took upon them the war, who went out in the host, —and all the [rest of the] assembly.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 Then shalt thou levy a tribute unto Yahweh—from the men of war, who went forth in the host, one living thing, out of five hundred, —of the human beings, and of the herd, and of the asses and of the flock:
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 out of their half, shall ye take [them], —and thou shall give [them] unto Eleazar the priest as a heave-offering unto Yahweh.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 And out of the half allotted to the sons of Israel, shalt thou take one allotted portion out of fifty of the human beings, of the herd, of the asses and of the flock of all the cattle, —and shalt give them unto the Levites, who keep the charge of the habitation of Yahweh.
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 And Moses and Eleazar the priest did, —As Yahweh commanded Moses.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 And it came to pass that the booty, over and above the prey which the people of the host had seized, was, —of the flock, six hundred and seventy-five thousand;
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 and, of the herd, seventy-two thousand;
Ngʼombe 72,000,
34 and, of the asses, sixty-one thousand;
abulu 61,000,
35 and, of the human persons, even of the woman-kind who had not cohabited with man, —all the persons, thirty-two thousand.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 And the half, the share of them who had gone forth in the host, was, —the number of the flock—three hundred and thirty-seven thousand and five hundred;
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 and so, the tribute unto Yahweh, out of the flock, was—six hundred and seventy-five;
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 and the herd, thirty-six thousand, —and the tribute of them unto Yahweh—seventy-two;
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 and the asses, thirty thousand and five hundred, —and the tribute of them unto Yahweh, sixty-one;
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 and the human persons, sixteen thousand, —and the tribute of them unto Yahweh, thirty-two persons.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 And Moses gave the tribute—the heave-offering of Yahweh, unto Eleazar the priest, —As Yahweh commanded Moses.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 And, of the half, allotted unto the sons of Israel, —which Moses halved away from the men who had gone out in the host,
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 the half allotted unto the assembly, was—of the flock, three hundred and thirty-seven thousand, and five hundred;
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 and, of the herd, six and thirty thousand;
ngʼombe 36,000,
45 and, of asses, thirty thousand and five hundred;
abulu 30,500,
46 and, human persons, sixteen thousand.
anthu 16,000.
47 So then Moses took—out of the half belonging to the sons of Israel the allotted portion one out of fifty, of the human beings and of the beasts, —and gave them unto the Levites, the keepers of the charge of the habitation of Yahweh, As Yahweh commanded Moses.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Then came near unto Moses the officers who belonged unto the thousands of the host, —the princes of thousands and the princes of hundreds;
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 and said unto Moses, Thy servants have reckoned up the sum of the men of war who are in our hand, —and there is not missed from among us, a man!
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 Therefore have we brought near an offering unto Yahweh, what, each man, hath found—articles of gold, ankle chains and bracelets, rings earrings and buckles, —to put a propitiatory-covering over our souls before Yahweh.
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 So Moses, and Eleazar the priest took the gold of them, —all the wrought articles.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 And all the gold of the heave-offering which they offered up unto Yahweh, was—sixteen thousand seven hundred and fifty shekels, —of the princes of thousands, and of the princes of hundreds.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 The men of the host, had taken prey, each man for himself.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 So then Moses and Eleazar the priest took the gold of the princes of thousands, and hundreds, —and brought it into the tent of meeting, as a memorial for the sons of Israel before Yahweh.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

< Numbers 31 >