< Malachi 1 >

1 The oracle of the word of Yahweh, unto Israel, —by the hand of Malachi.
Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
2 I have loved you, saith Yahweh, and yet ye say, Wherein hast thou loved us? Is not Esau, brother, to Jacob? enquireth Yahweh, Yet have I loved Jacob,
Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
3 And, Esau, have I hated, — and made his mountains a desolation, and his inheritance [a dwelling] for the jackals of the wilderness.
koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
4 Whereas Edom, may say, We are laid waste, but we will again build the desolate places, Thus, saith Yahweh of hosts, They, may build, but, I, will pull down, — and men shall call them, The Boundary of Lawlessness, and, The people with whom Yahweh hath indignation unto times age-abiding;
Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
5 And, your own eyes, shall see, —and, ye yourselves, shall say, Yahweh, be magnified, beyond the boundary of Israel.
Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
6 A son, will honour a father, and, a servant, his lord, — If then, a father, I am, where is mine honour? And, if, a lord, I am, where is my reverence? saith Yahweh of hosts— to you, ye priests, who despise my Name, and yet say, Wherein have we despised thy Name?
“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
7 In bringing near upon mine altar, polluted food, while yet ye say, Wherein have we polluted thee? Because ye say, As for the table of Yahweh, a thing to be despised, it is;
“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
8 And when ye bring near the blind as a sacrifice, [saying] —No harm! or when ye bring near the lame or the sick [saying] —No harm! Offer it, I pray you, unto thy pasha, Will he accept thee? or lift up thy countenance? saith Yahweh of hosts.
Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Now, therefore, pacify, I pray you, the face of GOD, that he may grant us favour, —at your hands, hath this come to pass, Will he lift up the countenances, of any of you? saith Yahweh of hosts.
“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
10 Who is there, even among you, that will shut the doors, so as not to set light to mine altar, for nothing? I can take no pleasure in you, saith Yahweh of hosts, and, your present, can I not accept at your hand.
“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
11 For, from the rising of the sun, even unto the going in thereof, great is my Name among the nations, and, in every place, incense, is offered to my Name, and a pure present, —for great is my Name among the nations, saith Yahweh of hosts.
Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 But ye are profaning me, — in that ye say, As for the table of the Lord, polluted it is, and, as for his produce, contemptible is his food.
“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
13 And ye have said, Lo! what a weariness! And ye have snuffed at Me, saith Yahweh of hosts, and have brought in the torn and the lame and the sick, thus have ye brought the present, — Could I accept it at your hand? saith Yahweh.
Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
14 But accursed is he that defraudeth, who, when there is in his flock a male, yet voweth and sacrificeth a corrupt thing to the Lord, for, a great king, am I, saith Yahweh of hosts, and, my Name, is revered among the nations.
“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”

< Malachi 1 >