< Hosea 4 >

1 Hear the word of Yahweh, ye sons of Israel, —that, a controversy, hath Yahweh with the inhabitants of the land, because there is no faithfulness, nor lovingkindness, nor knowledge of God, in the land:
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Cursing and lying, and killing and stealing, and committing adultery, have broken forth, and, blood-shedding, unto blood-shedding, doth extend.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 For this cause, shall the land mourn, and everyone who dwelleth therein shall languish, with the wild beast of the field and with the bird of the heavens, —moreover also, the fishes of the sea, shall be withdrawn.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 Howbeit let, no man, contend, nor let him rebuke another, —since, thy people, are as they who contend against a priest:
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 So shouldst thou stumble in the daytime, and even the prophet stumble with thee, in the night, —and I should destroy thine own mother.
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 My people, are destroyed, for lack of knowledge, —Because, thou, hast rejected knowledge, therefore will I reject thee from ministering as priest unto me, and, because thou hast forgotten the law of thy God, I also, will forget thy children.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 As they were magnified, so, they sinned against me, —My glory—for what was contemptible, did they exchange.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 The sin of my people, they do eat, —and. unto their iniquity, lift they up every man his desire.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 So doth it come to be—like people, like priest, —therefore will I visit upon him his ways, and, his doings, will I bring back to him;
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 And they shall eat, and not be satisfied, they have encouraged unchastity, yet have not been making increase, —for unto, Yahweh, have they left off giving heed: —
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 Unchastity, and wine, and new wine, take away the heart.
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 My people, of their Wood, do ask, —Let, their Staff, then tell them, —for, the spirit of unchastity, hath led them astray, and they have unchastely departed from under their God.
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 On the headlands of the mountains, they sacrifice, and, on the hills, burn they incense, under oak and poplar and terebinth, because, pleasant, is the shade thereof: For this cause, do your daughters, become unchaste, and, your brides, commit adultery.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 I do not bring punishment upon your daughters when they become unchaste, nor upon your brides, when they commit adultery, for, the men themselves, with unchaste women, do seclude themselves, and, with the common women of the shrine, do offer sacrifice, —and, a people who will not discern, must be ruined.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 Though unchaste art thou, O Israel, let not Judah, become guilty, neither let them enter Gilgal, nor go up to Beth-aven, and [then] swear, By the life of Yahweh!
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 For, as a heifer that is stubborn, hath Israel, been stubborn, —Now, can Yahweh, turn them out to pasture, like a young ram in a wide place?
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Mated with idols, is Ephraim, let him alone.
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 Their drinking-bout, having passed, —they became, unchaste, they loved wildly, a contempt, became her great men.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 The wind hath bound her up in its wings, —that they may be ashamed, because of their sacrifices.
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

< Hosea 4 >