< Ezekiel 6 >

1 Then came the word of Yahweh. unto me saying,
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 Son of man, Set thy face against the mountains of Israel, — and prophesy unto them;
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
3 and say, Ye mountains of Israel, hear ye the word of My Lord Yahweh, — Thus saith My Lord, Yahweh- To the mountains and to the hills to the hollows and to the valleys, - Behold me! I, am bringing upon you a sword, And I will destroy your high places;
kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
4 And your altars shall be laid waste, And your sun-pillars shall be broken in pieces, — And I will cause your slain to fall before your manufactured gods;
Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
5 And I will lay the carcases of the sons of Israel before their manufactured gods, — And will scatter your bones round about your altars.
Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
6 In all your dwelling-places, The cities, shall be laid waste, and, The high places, shall be made desolate, To the end your altars may be laid waste and become desolate. And your manufactured gods be broken in pieces and cease, And your sun-pillars be cut down, And your handiworks be abolished.
Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
7 And the slain shall fall in your midst, So shall ye know that I am Yahweh.
Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
8 Yet will I leave a remnant: In that ye shall have such as are escaped of the sword throughout the nations, when ye are scattered throughout the lands.
“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
9 Then shall they who have escaped of you remember me, among the nations whither they have been carried captive, In that I have broken their adulterous heart, which hath turned aside from me, And their eyes which have adulterously gone after their manufactured gods, So shall they become loathsome in their own sight, for the wicked things which they have done in all their abominations.
Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
10 Then shall they know that, I, Yahweh, —not in vain, had threatened to bring upon them this calamity.
Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
11 Thus saith My Lord. Yahweh, Smite with thy hand, and stamp with thy foot and say, Alas! regarding all the wicked abominations of the house of Israel, —in that by sword, by famine, and by pestilence, shall they fall:
“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
12 He that is far off by pestilence, shall die and He that is near by the sword, shall fall, and He that is left and is besieged by the famine, shall die; Thus will I make an end of mine indignation against them.
Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
13 So shall ye know that I, am Yahweh, In that their slain are in the midst of their manufactured gods, on every side of their altars, — Upon every high hill In all the tops of the mountains and Under every green tree and Under every tangled oak, The place where they offered a satisfying odour to all their manufactured gods.
Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
14 Thus will I stretch out my hand upon them, and make the land a greater waste and devastation than the desert toward Diblah throughout all their dwelling-places, - And they shall know that, I, am Yahweh.
Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 6 >