< Exodus 6 >

1 Then said Yahweh unto Moses, Now, shalt thou see, what I will do to Pharaoh, for with a strong hand, shall he let them go, and with a strong hand, shall he drive them out from his land.
Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
2 And God spake unto Moses, —and said unto him, I, am Yahweh:
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
3 I appeared, therefore, unto Abraham unto Isaac, and unto Jacob, as GOD Almighty, —although, by my name Yahweh was I not made known to them;
Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
4 Moreover also I established my covenant with them, to give them the land of Canaan, —even the land of their sojournings wherein they sojourned.
Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
5 Moreover also, I heard the groaning of the sons of Israel, whom the Egyptians, were holding in servitude, So then I remembered my covenant.
Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
6 Therefore say thou to the sons of Israel-I, am Yahweh, Therefore will I bring you forth from under the burdens of Egypt, And will deliver you out of their service, And will redeem you with a stretched-out arm, and with great judgments;
“Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
7 And will take you to myself for a people, And will become your God, —And ye shall know that, I Yahweh, am your God, who brought you forth from under the burdens of Egypt:
Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
8 And I will bring you into the land as to which I uplifted my hand to give it to Abraham, to Isaac, and to Jacob, —and will give it to you as an inheritance: I, am Yahweh.
Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
9 And Moses spake thus unto the sons of Israel, but they hearkened not unto Moses, through shortness of spirit, and through hard service.
Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
10 And Yahweh spake unto Moses saying:
Kenaka Yehova anati kwa Mose,
11 Go in speak unto Pharaoh king of Egypt, that he let the sons of Israel go out of his land.
“Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
12 And Moses spake before Yahweh, saying, —Lo! the sons of Israel have not hearkened unto me, how then shall Pharaoh, hear, I, also being of uncircumcised lips.
Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
13 Thus then did Yahweh speak unto Moses and unto Aaron, yea he gave them a charge unto the sons of Israel, and unto Pharaoh king of Egypt, for the bringing forth of the sons of Israel out of the land of Egypt.
Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
14 These, are the heads of their ancestral house: The sons of Reuben the first-born of Israel, Hanoch and Pallu, Hezron and Carmi. These are the families of, Reuben.
Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
15 And, the sons of Simeon, Jemuel and Jamin and Ohad and Jachin and Zohar, and Shaul the son of a Canaanitess. These, are the families of, Simeon.
Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
16 And, these, are the names of the sons of Levi by their generations, Gershon, and Kohath and Merari, And, the years of the life of Levi, were a hundred and thirty-seven years.
Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
17 The sons of Gershon, Libni and Shimei by their families.
Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
18 And the sons of Kohath, Amram and Izhar, and Hebron and Uzziel. And the years of the life of Kohath, were a hundred and thirty-three years.
Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
19 And the sons of Merari, Mahli and Mushi. These, are the families of the Levites by their generations.
Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
20 So then, Amram took Jochebed, his father’s sister to himself to wife, and she bare to him—Aaron and Moses. And, the years of the life of Amram, were a hundred and thirty-seven.
Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
21 And the sons of Izhar, Korah and Nepheg, and Zichri.
Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
22 And the sons of Uzziel, Mishael and Elzaphan, and Sithri.
Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
23 And Aaron took Elisheba, daughter of Amminadab, sister of Nahshon, to himself to wife, —and she bare to him—Nadab, and Abihu, Eleazar, and Ithamar.
Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
24 And the sons of Korah, Assir and Elkanah, and Abiasaph. These are the families of the Korahites.
Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
25 And Eleazar, son of Aaron took to himself [one] of the daughters of Putiel, to himself to wife, and she bare to him Phinehas. These, are the heads of the fathers of the Levites by their families.
Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
26 The same, Aaron and Moses, —to whom said Yahweh, Bring ye forth the sons of Israel out of the land of Egypt, according to their hosts:
Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
27 They who were to speak unto Pharaoh king of Egypt, to bring forth the sons of Israel out of Egypt: The same, Moses and Aaron.
Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
28 Thus came it to pass, that on a certain day, Yahweh spake unto Moses in the land of Egypt.
Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
29 So then Yahweh spake unto Moses, saying—I, am Yahweh: Speak thou unto Pharaoh king of Egypt, all that, I, am speaking unto thee.
anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
30 And Moses said before Yahweh, —Lo! I, am of uncircumcised lips, how then will Pharaoh hearken unto me?
Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”

< Exodus 6 >