< Colossians 2 >

1 For I desire you to know, how great a contest I am having—in behalf of you, and of those in Laodicea, and as many as have not seen my face in the flesh;
Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso.
2 In order that their hearts may be encouraged, being knit together in love, even unto all the riches of the full assurance of their understanding, unto a personal knowledge of the sacred secret of God, —Christ:
Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu.
3 In whom are all the treasures of wisdom and knowledge hidden away.
Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso.
4 This I say, in order that, no one, may be reasoning, you, aside with plausible discourse;
Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake.
5 For, though, indeed, in the flesh, I am absent, yet, in the spirit, with you, I am—rejoicing, and beholding your order and the solid firmness of your Christ-ward faith.
Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
6 As therefore ye have accepted the Anointed Jesus as your Lord, in him, be walking, —
Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo.
7 Rooted, and being built up, in him, and making yourselves sure in your faith, even as ye have been taught, —surpassing therein with thanksgiving.
Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
8 Be taking heed, lest there shall be anyone leading, you, off as a spoil, through means of their philosophy, and an empty deceit, —according to the instruction of men, according to the first principles of the world, —and not according to Christ:
Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
9 Because, in him, dwelleth all the fullness of the Godhead, bodily,
Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu.
10 And ye are, in him, filled full, —Who, is the head of all principality and authority,
Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse.
11 In whom, ye have also been circumcised with a circumcision not done by hand, in the despoiling of the body of flesh, in the circumcision of the Christ, —
Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija.
12 Having been buried together with him in your immersion, wherein also ye have been raised together, through your faith in the energising of God—Who raised him from among the dead.
Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
13 And, as for you—who were, dead, by your offences and by the uncircumcision of your flesh, he hath brought you to life together with him, —having in favour forgiven us all our offences,
Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse.
14 Having blotted out the handwriting against us by the decrees, which was hostile to us, —and hath taken away, the same, out of the midst, nailing it up to the cross:
Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda.
15 Spoiling the principalities and the authorities, he made of them an open example, celebrating a triumph over them thereby.
Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
16 Let no one, therefore, be judging, you, —in eating and in drinking, or in respect of feast, or new moon, or sabbath, —
Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata.
17 Which are a shadow of the things to come, whereas, the body, is of the Christ.
Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu.
18 Let, no one, against you, be arbitrating, however wishful, —in respect of lowliness of mind, and of a religious observance of the messengers: upon what things he hath seen, taking his stand, in vain, puffed up by his carnal mind, —
Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu.
19 And not holding fast the head: from which, all the body, through means of its joints and uniting bands, receiving supply, and connecting itself together, groweth with the growth of God.
Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
20 If ye have died, together with Christ, from the first principles of the world, why, as though alive in the world, are ye submitting to decrees, —
Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa:
21 Do not handle, nor taste, nor touch; —
“Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?”
22 Which things are all for decay in the using up; —according to the commandments and teachings of men?
Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe.
23 The which things, indeed, though they have, an appearance, of wisdom, in self-devised religious observance, and lowliness of mind, [and] ill-treatment of body, are, in no honourable way, unto a satisfying of the flesh.
Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

< Colossians 2 >