< 2 Samuel 23 >

1 Now, these, are the last words of David, —The oracle of David, son of Jesse, Yea the oracle of The man raised up on high, The Anointed of the God of Jacob, the Delight of the Songs of Israel:
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 The Spirit of Yahweh, spake in me, —And, his word, was on my tongue;
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 Said the God of Israel, Unto me, spake the Rock of Israel: —One Ruling over Men, A Righteous One, ruling in the reverence of God,
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 Is even as the light of the morning when ariseth the sun, —A morning, without clouds, [As] from brightness, [and] from rain, the fresh shoots out of the earth.
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 When, not so, was my house with GOD, Then, a covenant age-abiding, he appointed me, Ordered in all things and guarded, Now that it is all my salvation and all my desire, Will he not make it shoot forth?
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 But, as for the abandoned, like thorns to be tossed away are they all, —For, not with the hand, can they be taken;
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 But, the man that would touch them, Must fence himself with iron, and the shaft of a spear, —Then, with fire, shall they be, consumed, on the spot!
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 These, are the names of the mighty men, who belonged to David, —The president a Tachmonite head of the charioteers, the same, was Adino the Eznite, for eight hundred, slain at one time.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 And, after him, Eleazar son of Dodo, son of Ahohi, —in the hero-class of mighty men, with David, when they reproached the Philistines, they were gathered together there to battle, but the men of Israel had gone up;
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 he, however, arose and smote among the Philistines until his hand was weary, and his hand clave unto his sword, so Yahweh wrought a great victory on that day, —the people, coming back after him, only to strip the slain.
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 And, after him, Shammah son of Agee, the Hararite, —and, when the Philistines were gathered together into a troop, there being at hand an allotment of field-land full of lentils, but, the people, having fled from the face of the Philistines,
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 then took he his stand in the midst of the allotment, and defended it, and smote the Philistines, —and Yahweh wrought a great victory.
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 And three of the thirty chiefs descended, and came in, towards harvest, unto David, unto the cave of Adullam, —although, a troop of Philistines, were encamped in the vale of Rephaim;
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 and, David, then was in a stronghold, —and, a garrison of Philistines, was then in Bethlehem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 And David longed, and said, —Who will give me to drink water out of the well of Bethlehem, that is within the gate?
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 And the three mighty men brake through the camp of Philistines, and drew water out of the well of Bethlehem, that was within the gate, and bare it, and brought it in unto David, —yet would he not drink, but poured it out unto Yahweh,
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 and said—Be it far from me, O Yahweh, that I should do this! is it not the blood of the men who went with their lives [in their hands]? So he would not drink it. These things, did the three mighty men.
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 And. Abishai brother of Joab son of Zeruiah, he, was chief of three, in that he brandished his spear against three hundred whom he slew; and, he, had a name among three.
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 Was he not most honourable, of the three, and so became their captain? Nevertheless, unto the three, he attained not.
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 Benaiah also, son of Jehoiadah, son of an active man, hero of many a deed, a man of Kabzeel, he, smote the two sons of Ariel of Moab, he, also went down and smote a lion in the midst of a pit, on a day of snow;
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 he, also smote an Egyptian, who was of valiant bearing, and, in the hand of the Egyptian, was a spear, but he went down unto him with a staff, —and wrested the spear out of the hand of the Egyptian, and slew him with his own spear.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 These things, did Benaiah son of Jehoiada, and, he, had a name among three mighty men.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 He was the most honourable, of thirty, although, unto the three, he attained no, —so David added him to his council.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Asahel, brother of Joab, was among the thirty, —Elhanan, son of Dodo, of Bethlehem;
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Shammah, the Harodite; Elika, the Harodite;
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Helez, the Paltite, Ira, son of Ikkesh, the Tekoite;
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Abiezer, the Anathothite, Mebunnai, the Hushathite;
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Zalmon, the Ahohite, Maharai, the Netophathite;
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Heleb, son of Baanah, the Netophathite, —Ittai, son of Ribai, of Gibeah, of the sons of Benjamin;
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Benaiah, a Pirathonite, Hiddai, of the torrents of Gaash;
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abi-albon, the Arbathite, Azmaveth, the Barhumite;
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliahba, the Shaalbonite, (Of) the sons of Jashen, Jonathan;
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 Shammah, the Hararite, Ahiam, son of Sharar, the Ararite;
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphelet, son of Ahasbai, son of the Maacathite. Eliam, son of Ahithophel, the Gilonite.
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 Hezro, the Carmelite, Paarai, the Arbite;
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Igal, son of Nathan, of Zobah, Bani, the Gadite;
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Zelek, the Ammonite, —Naharai, the Beerothite, armour bearers to Joab son of Zeruiah;
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Ira, the Ithrite, Gareb, the Ithrite;
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Uriah, the Hittite, In all, thirty and seven.
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.

< 2 Samuel 23 >