< 2 Samuel 1 >

1 And so it was, after the death of Saul, when David had returned from the smiting of the Amalekites, and David had abode in Ziklag two days,
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 yea so it was, on the third day, that lo! a man came out of the camp, from Saul, with his clothes rent, and earth upon his head, —and so it was, when he came in unto David, that he fell to the earth, and did homage.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 And David said unto him, From whence comest thou? And he said unto him, Out of the camp of Israel, am I escaped.
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 And David said unto him—How turned out the matter? tell me, I pray thee. And he said—The people have fled from the battle, yea moreover, many, of the people have fallen, and died, Yea moreover, Saul, and Jonathan his son, are dead.
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 Then said David unto the young man who was telling him, —How knowest thou that Saul and Jonathan his son are dead?
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 And the young man who was telling him said, It, so happened, that I was on Mount Gilboa, when lo! Saul, leaning upon his spear, and lo! the chariots and horsemen, hotly pursued him;
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 so he turned behind him, and saw me, —and cried out unto me, and I said, Behold me!
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 And he said unto me, Who art thou? And I said unto him, An Amalekite, am I.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 And he said unto me, I pray thee, take thy stand by me, and put me to death, for the cramp hath seized me, —even for as long as my life shall be in me.
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 So I took my stand by him, and put him to death, for I perceived that he could not survive his fall, —so I took the crown that was on his head, and the bracelet that was on his arm, and have brought them in unto my lord, here.
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 Then David took hold of his clothes, and rent them, —yea moreover, [so did] all the men who were with him.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 And they lamented aloud, and wept, and fasted until the evening, —for Saul, and for Jonathan his son, and for the people of Yahweh, and for the house of Israel, because they had fallen by the sword.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 And David said unto the young man who was telling him, Whence art thou? And he said, Son of a sojourner—an Amalekite, am I.
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 And David said unto him, —How wast thou not afraid to thrust forth thy hand, to destroy the Anointed of Yahweh?
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 So David called one of the young men, and said, —Go near—fall upon him. And he smote him, that he died.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 And David said unto him, Thy blood, be upon thine own head, —for, thine own mouth, hath testified against thee, saying, I myself, put to death the Anointed of Yahweh.
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 Then chanted David this dirge, —over Saul and over Jonathan his son;
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 and he thought to teach the sons of Judah [the song of] the Bow, —lo! it is written in the Book of the Upright: —
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 The beauty of Israel! on thy high plumes—slain! How have fallen—the mighty!
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Do not tell it in Gath, Do not publish it in the streets of Ashkelon, —lest the daughters of the Philistines rejoice, lest the daughters of the Uncircumcised triumph.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 Ye mountains in Gilboa! Be there neither dew nor rain upon you, nor fields of offerings, —for, there, were cast away, the shields of the mighty, The shield of Saul, unanointed with oil.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 From the blood of the slain, from the fat of the mighty, the bow of Jonathan ne’er drew back, —and, the sword of Saul, ne’er returned, empty.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saul and Jonathan, delightfully loving in their lives, even, in their death, were not divided, —Beyond eagles, were they swift, beyond lions, were they strong!
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 Ye daughters of Israel! For Saul, weep ye, —who clothed you in crimson, [decked] with lovely things, who hung ornaments of gold on your apparel!
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 How have fallen the mighty, in the midst of the battle! Jonathan, on thy high places, slain!
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 I am distressed for thee, my brother, Jonathan! Delightful to me, exceedingly, —Wonderful, was thy love to me, passing the love of women.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 How have fallen the mighty, and perished the weapons of war!
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuel 1 >