< 2 Chronicles 7 >

1 Now, when Solomon had made an end of praying, Fire, came down out of the heavens, and consumed the ascending-offering and the sacrifices, —and, the glory of Yahweh, filled the house;
Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
2 so that the priests could not enter into the house of Yahweh, —because the glory of Yahweh filled the house of Yahweh;
Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
3 and, all the sons of Israel, seeing the descending of the fire and the glory of Yahweh upon the house, then knelt they down with their faces toward the ground, upon the pavement, and bowed themselves in prostration, and gave thanks unto Yahweh, For he is good, For, age-abiding, is his lovingkindness.
Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
4 And, the king and all the people, were offering sacrifice before Yahweh.
Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
5 And King Solomon offered a sacrifice—of oxen, twenty-two thousand, and of sheep, a hundred and twenty thousand, —and so the king and all the people, dedicated the house of God;
Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
6 while, the priests, over their charges, were standing, the Levites also, with the instruments for the songs of Yahweh, which David the king had made, for giving thanks unto Yahweh, For, age-abiding, is his lovingkindness, when David offered praise by their means, —and, the priests, kept on blowing trumpets over against them, while, all Israel, were standing.
Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
7 And Solomon hallowed the middle of the court that was before the house of Yahweh, for he offered there the ascending-sacrifices, and the fat portions of the peace-offerings, —because, the altar of bronze which Solomon had made, was not able to receive the ascending-sacrifice and the meal-offering and the fat portions.
Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
8 And Solomon made a festival—at that time—for seven days, and all Israel with him, an exceeding great convocation, —from the entering in of Hamath, unto the ravine of Egypt.
Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
9 And they made, on the eighth day, a closing feast, —because, the dedication of the altar, they had kept seven days and a festival seven days.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
10 And, on the twenty-third of the seventh month, he sent the people away to their own homes, —rejoicing and glad in heart, over the goodness which Yahweh had performed unto David and unto Solomon, and unto Israel his people.
Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
11 Thus Solomon finished the house of Yahweh, and the house of the king, —and, all that had come in upon the heart of Solomon, to do in the house of Yahweh and in his own house, he prosperously executed.
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
12 Then appeared Yahweh unto Solomon by night, —and said to him, I have heard thy prayer, and have made choice of this place for myself, as a house of sacrifice: —
Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
13 If I shut up the heavens that there be no rain, or if I lay command on the locust, to devour the land, —or if I send pestilence, amongst my people:
“Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
14 if my people upon whom my Name is called shall humble themselves, and pray and seek my face, and turn from their wicked ways, then will, I myself, hear out of the heavens, and forgive their sin, and heal their land.
ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
15 Now, mine eyes, shall be open, and, mine ears, attent, —to the prayer of this place.
Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
16 Now, therefore, have I chosen and hallowed this house, that my Name may be there, unto times age-abiding, —and mine eyes and my heart shall he there, all the days.
Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
17 Thou, therefore, if thou wilt walk before me, as David thy father walked, even to do according to all that I have commanded thee, —and, my statutes and regulations, thou wilt observe,
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
18 then will I establish the throne of thy kingdom, —according as I covenanted to David thy father, saying—There shall not fail thee a man, to rule over Israel.
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
19 But, if, ye yourselves, shall turn away, and forsake my statutes and my commandments, which I have set before you, —and shall go and serve other gods, and bow down to them,
“Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
20 then will I root you out from off the soil, which I have given to you, and, this house, which I have hallowed for my Name, will I cast off from before my face, —and will appoint it for a by-word and a mockery, among all the peoples;
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
21 and, this house which hath been renowned, all that pass by near it, shall be astonished, —and say, Wherefore hath Yahweh done, thus and thus, to this land, and to this house?
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
22 And men shall say, Because they forsook Yahweh the God of their fathers, who brought them up out of the land of Egypt, and laid hold of other gods, and bowed down to them, and served them, for this cause, hath he brought upon them, all this calamity.
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”

< 2 Chronicles 7 >