< Psalms 58 >

1 For the Chief Musician; [set to] Al-tashheth. [A Psalm] of David: Michtam. Do ye indeed in silence speak righteousness? do ye judge uprightly, O ye sons of men?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Yea, in heart ye work wickedness; ye weigh out the violence of your hands in the earth.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 The wicked are estranged from the womb: they go astray as soon as they be born, speaking lies.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Their poison is like the poison of a serpent: [they are] like the deaf adder that stoppeth her ear;
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Which hearkeneth not to the voice of charmers, charming never so wisely.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Break their teeth, O God, in their mouth: break out the great teeth of the young lions, O LORD.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Let them melt away as water that runneth apace: when he aimeth his arrows, let them be as though they were cut off.
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 [Let them be] as a snail which melteth and passeth away: [like] the untimely birth of a woman, that hath not seen the sun.
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Before your pots can feel the thorns, he shall take them away with a whirlwind, the green and the burning alike.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 The righteous shall rejoice when he seeth the vengeance: he shall wash his feet in the blood of the wicked.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 So that men shall say, Verily there is a reward for the righteous: verily there is a God that judgeth in the earth.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

< Psalms 58 >