< Psalms 48 >

1 A Song; a Psalm of the sons of Korah. Great is the LORD, and highly to be praised, in the city of our God, in his holy mountain.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Beautiful in elevation, the joy of the whole earth, is mount Zion, [on] the sides of the north, the city of the great King.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 God hath made himself known in her palaces for a refuge.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 For, lo, the kings assembled themselves, they passed by together.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 They saw it, then were they amazed; they were dismayed, they hasted away.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Trembling took hold of them there; pain, as of a woman in travail.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 With the east wind thou breakest the ships of Tarshish.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 As we have heard, so have we seen in the city of the LORD of hosts, in the city of our God: God will establish it for ever. (Selah)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 We have thought on thy lovingkindness, O God, in the midst of thy temple.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 As is thy name, O God, so is thy praise unto the ends of the earth: thy right hand is full of righteousness.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Let mount Zion be glad, let the daughters of Judah rejoice, because of thy judgments.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Walk about Zion, and go round about her: tell the towers thereof.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Mark ye welt her bulwarks, consider her palaces; that ye may tell it to the generation following.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 For this God is our God for ever and ever: he will be our guide [even] unto death.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Psalms 48 >