< Psalms 139 >

1 For the Chief Musician. A Psalm of David. LORD, thou hast searched me, and known [me].
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 Thou knowest my downsitting and mine uprising, thou understandest my thought afar off.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 Thou searchest out my path and my lying down, and art acquainted with all my ways.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 For there is not a word in my tongue, but, lo, O LORD, thou knowest it altogether.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 Thou hast beset me behind and before, and laid thine hand upon me.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 [Such] knowledge is too wonderful for me; it is high, I cannot attain unto it.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Whither shall I from thy spirit? or whither shall I flee from thy presence?
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 If I ascend up into heaven, thou art there: if I make my bed in Sheol, behold, thou art there. (Sheol h7585)
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
9 If I take the wings of the morning, and dwell in the uttermost parts of the sea;
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 Even there shall thy hand lead me, and thy right hand shall hold me.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 If I say, Surely the darkness shall overwhelm me, and the light about me shall be night;
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 Even the darkness hideth not from thee, but the night shineth as the day: the darkness and the light are both alike [to thee].
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 For thou hast possessed my reins: thou hast covered me in my mother’s womb.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 I will give thanks unto thee; for I am fearfully and wonderfully made: wonderful are thy works; and that my soul knoweth right well.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 My frame was not hidden from thee, when I was made in secret, and curiously wrought in the lowest parts of the earth.
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Thine eyes did see mine unperfect substance, and in thy book were all [my members] written, which day by day were fashioned, when as yet there was none of them.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 How precious also are thy thoughts unto me, O God! how great is the sum of them!
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 If I should count them, they are more in number than the sand: when I awake, I am still with thee.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 Surely thou wilt slay the wicked, O God: depart from me therefore, ye bloodthirsty men.
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 For they speak against thee wickedly, and thine enemies take [thy name] in vain.
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 Do not I hate them, O LORD, that hate thee? and am not I grieved with those that rise up against thee?
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 I hate them with perfect hatred: I count them mine enemies.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Search me, O God, and know my heart: try me and know my thoughts:
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 And see if there be any way of wickedness in me, and lead me in the way everlasting.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

< Psalms 139 >