< Proverbs 13 >

1 A WISE son [heareth] his father’s instruction: but a scorner heareth not rebuke.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 A man shall eat good by the fruit of his mouth: but the soul of the treacherous [shall eat] violence.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 He that guardeth his mouth keepeth his life: [but] he that openeth wide his lips shall have destruction.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 The soul of the sluggard desireth, and hath nothing: but the soul of the diligent shall be made fat.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 A righteous man hateth lying: but a wicked man is loathsome, and cometh to shame.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Righteousness guardeth him that is upright in the way: but wickedness overthroweth the sinner.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 There is that maketh himself rich, yet hath nothing: there is that maketh himself poor, yet hath great wealth.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 The ransom of a man’s life is his riches: but the poor heareth no threatening.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 The light of the righteous rejoiceth: but the lamp of the wicked shall be put out.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 By pride cometh only contention: but with the well advised is wisdom.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Wealth gotten by vanity shall be diminished: but he that gathereth by labour shall have increase.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Hope deferred maketh the heart sick: but when the desire cometh, it is a tree of life.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Whoso despiseth the word bringeth destruction on himself: but he that feareth the commandment shall be rewarded.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 The law of the wise is a fountain of life, to depart from the snares of death.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Good understanding giveth favour: but the way of the treacherous is rugged.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Every prudent man worketh with knowledge: but a fool spreadeth out folly.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 A wicked messenger falleth into evil: but a faithful ambassador is health.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Poverty and shame [shall be to] him that refuseth correction: but he that regardeth reproof shall be honoured.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 The desire accomplished is sweet to the soul: but it is an abomination to fools to depart from evil.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Walk with wise men, and thou shalt be wise: but the companion of fools shall smart for it.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Evil pursueth sinners: but the righteous shall be recompensed with good.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 A good man leaveth an inheritance to his children’s children; and the wealth of the sinner is laid up for the righteous.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Much food [is in] the tillage of the poor: but there is that is destroyed by reason of injustice.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 He that spareth his rod hateth his son: but he that loveth him chasteneth him betimes.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 The righteous eateth to the satisfying of his soul: but the belly of the wicked shall want.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Proverbs 13 >