< Numbers 1 >

1 And the LORD spake unto Moses in the wilderness of Sinai, in the tent of meeting, on the first day of the second month, in the second year after they were come out of the land of Egypt, saying,
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 Take ye the sum of all the congregation of the children of Israel, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, every male, by their polls;
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 from twenty years old and upward, all that are able to go forth to war in Israel, thou and Aaron shall number them by their hosts.
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 And with you there shall be a man of every tribe; every one head of his fathers’ house.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 And these are the names of the men that shall stand with you: of Reuben; Elizur the son of Shedeur.
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 Of Simeon; Shelumiel the son of Zurishaddai.
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 Of Judah; Nahshon the son of Amminadab.
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 Of Issachar; Nethanel the son of Zuar.
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 Of Zebulun; Eliab the son of Helon.
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 Of the children of Joseph: of Ephraim; Elishama the son of Ammihud: of Manasseh; Gamaliel the son of Pedahzur.
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 Of Benjamin; Abidan the son of Gideoni.
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 Of Dan; Ahiezer the son of Ammishaddai.
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 Of Asher; Pagiel the son of Ochran.
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 Of Gad; Eliasaph the son of Deuel.
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 Of Naphtali; Ahira the son of Enan.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 These are they that were called of the congregation, the princes of the tribes of their fathers; they were the heads of the thousands of Israel.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 And Moses and Aaron took these men which are expressed by name:
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 And they assembled all the congregation together on the first day of the second month, and they declared their pedigrees after their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, by their polls.
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 As the LORD commanded Moses, so he numbered them in the wilderness of Sinai.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 And the children of Reuben, Israel’s firstborn, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, by their polls, every male from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 those that were numbered of them, of the tribe of Reuben, were forty and six thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Of the children of Simeon, their generations, by their families, by their fathers’ houses, those that were numbered thereof, according to the number of the names, by their polls, every male from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 those that were numbered of them, of the tribe of Simeon, were fifty and nine thousand and three hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Of the children of Gad, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 those that were numbered of them, of the tribe of Gad, were forty and five thousand six hundred and fifty.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 Of the children of Judah, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 those that were numbered of them, of the tribe of Judah, were threescore and fourteen thousand and six hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 Of the children of Issachar, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 those that were numbered of them, of the tribe of Issachar, were fifty and four thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 Of the children of Zebulun, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 those that were numbered of them, of the tribe of Zebulun, were fifty and seven thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 Of the children of Joseph, [namely], of the children of Ephraim, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 those that were numbered of them, of the tribe of Ephraim, were forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 Of the children of Manasseh, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 those that were numbered of them, of the tribe of Manasseh, were thirty and two thousand and two hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 Of the children of Benjamin, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 those that were numbered of them, of the tribe of Benjamin, were thirty and five thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 Of the children of Dan, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 those that were numbered of them, of the tribe of Dan, were threescore and two thousand and seven hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 Of the children of Asher, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 those that were numbered of them, of the tribe of Asher, were forty and one thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 Of the children of Naphtali, their generations, by their families, by their fathers’ houses, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 those that were numbered of them, of the tribe of Naphtali, were fifty and three thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 These are they that were numbered, which Moses and Aaron numbered, and the princes of Israel, being twelve men: they were each one for his fathers’ house.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 So all they that were numbered of the children of Israel by their fathers’ houses, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war in Israel;
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 even all they that were numbered were six hundred thousand and three thousand and five hundred and fifty.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 But the Levites after the tribe of their fathers were not numbered among them.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 For the LORD spake unto Moses, saying,
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 Only the tribe of Levi thou shalt not number, neither shalt thou take the sum of them among the children of Israel:
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 but appoint thou the Levites over the tabernacle of the testimony, and over all the furniture thereof, and over all that belongeth to it: they shall bear the tabernacle, and all the furniture thereof; and they shall minister unto it, and shall encamp round about the tabernacle.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 And when the tabernacle setteth forward, the Levites shall take it down: and when the tabernacle is to be pitched, the Levites shall set it up: and the stranger that cometh nigh shall be put to death.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 And the children of Israel shall pitch their tents, every man by his own camp, and every man by his own standard, according to their hosts.
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 But the Levites shall pitch round about the tabernacle of the testimony, that there be no wrath upon the congregation of the children of Israel: and the Levites shall keep the charge of the tabernacle of the testimony.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 Thus did the children of Israel; according to all that the LORD commanded Moses, so did they.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

< Numbers 1 >