< Isaiah 27 >

1 In that day the LORD with his sore and great and strong sword shall punish leviathan the swift serpent, and leviathan the crooked serpent; and he shall slay the dragon that is in the sea.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 In that day: A vineyard of wine, sing ye unto it.
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 I the LORD do keep it; I will water it every moment: lest any hurt it, I will keep it night and day.
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 Fury is not in me: would that the briers and thorns were against me in battle! I would march upon them, I would burn them together.
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Or else let him take hold of my strength, that he may make peace with me; [yea], let him make peace with me.
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 In days to come shall Jacob take root; Israel shall blossom and bud: and they shall fill the face of the world with fruit.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Hath he smitten him as he smote those that smote him? or is he slain according to the slaughter of them that were slain by him?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 In measure, when thou sendest her away, thou dost contend with her; he hath removed [her] with his rough blast in the day of the east wind.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Therefore by this shall the iniquity of Jacob be purged, and this is all the fruit of taking away his sin; when he maketh all the stones of the altar as chalkstones that are beaten in sunder, [so that] the Asherim and the sun-images shall rise no more.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 For the defenced city is solitary, an habitation deserted and forsaken, like the wilderness: there shall the calf feed, and there shall he lie down, and consume the branches thereof.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 When the boughs thereof are withered, they shall be broken off; the women shall come, and set them on fire: for it is a people of no understanding; therefore he that made them will not have compassion upon them, and he that formed them will shew them no favour.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 And it shall come to pass in that day, that the LORD shall beat off [his fruit], from the flood of the River unto the brook of Egypt, and ye shall be gathered one by one, O ye children of Israel.
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 And it shall come to pass in that day, that a great trumpet shall be blown; and they shall come which were ready to perish in the land of Assyria, and they that were outcasts in the land of Egypt; and they shall worship the LORD in the holy mountain at Jerusalem.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

< Isaiah 27 >