< Psalms 25 >

1 A psalm of David. To you, O Lord, I lift up my heart: all the day I wait for you.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 In you I trust, put me not to shame; let not my foes exult over me.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 None will be shamed who wait for you, but shame will fall upon wanton traitors.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Make me, O Lord, to know your ways: teach me your paths.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 In your faithfulness guide me and teach me, for you are my God and my saviour.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Remember your pity, O Lord, and your kindness, for they have been ever of old.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Do not remember the sins of my youth; remember me in kindness, because of your goodness, Lord.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Good is the Lord and upright, so he teaches sinners the way.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 The humble he guides in the right, he teaches the humble his way.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 All his ways are loving and loyal to those who observe his charges and covenant.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Be true to your name Lord, forgive my many sins.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Who then is the person who fears the Lord? He will teach them the way to choose.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 They will live in prosperity, their children will inherit the land.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 The Lord gives guidance to those who fear him, and with his covenant he makes them acquainted.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 My eyes are ever toward the Lord, for out of the net he brings my foot.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Turn to me with your favour, for I am lonely and crushed
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 In my heart are strain and storm; bring me out of my distresses.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Look on my misery and trouble, and pardon all my sins,
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 look on my foes oh, so many! And their cruel hatred towards me.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Deliver me, keep me, and shame not one who takes refuge in you.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 May integrity and innocence preserve me, for I wait for you, O Lord.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Redeem Israel, O God, from all its distresses.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Psalms 25 >