< Matthew 26 >

1 When Jesus had finished teaching all of that, he said to his disciples,
Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake,
2 ‘You know that in two days time the Festival of the Passover will be here; and that the Son of Man is to be given up to be crucified.’
“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”
3 Then the chief priests and the elders of the people met in the house of the high priest, who was called Caiaphas,
Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,
4 and plotted together to arrest Jesus by stealth and put him to death;
ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha.
5 but they said, ‘Not during the Festival, or the people may riot.’
Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”
6 After Jesus had reached Bethany, and while he was in the house of Simon the leper,
Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate,
7 a woman came up to him with an alabaster jar of very costly perfume, and poured the perfume on his head as he sat at the table.
mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.
8 The disciples were indignant at seeing this. ‘What is this waste for?’ they exclaimed.
Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere?
9 ‘It could have been sold for a large sum, and the money given to poor people.’
Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”
10 ‘Why are you troubling the woman?’ Jesus said, when he noticed it. ‘For this is a beautiful deed that she has done to me.
Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
11 You always have the poor with you, but you will not always have me.
Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
12 In pouring this perfume on my body, she prepares me for my burial.
Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
13 I tell you, wherever, in the whole world, this good news is proclaimed, what this woman has done will be told in memory of her.’
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”
14 It was then that one of the Twelve, named Judas Iscariot, made his way to the chief priests,
Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe
15 and said ‘What are you willing to give me, if I betray Jesus to you?’ The Priests counted him out thirty pieces of silver as payment.
nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu.
16 So from that time Judas looked for an opportunity to betray Jesus.
Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.
17 On the first day of the Festival of the unleavened bread, the disciples came up to Jesus, and said, ‘Where do you wish us to make preparations for you to eat the Passover?’
Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”
18 ‘Go into the city to a certain man,’ he answered, ‘and say to him “The teacher says – My time is near. I will keep the Passover with my disciples at your house.”’
Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’”
19 The disciples did as Jesus directed them, and prepared the Passover.
Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.
20 In the evening Jesus took his place with the twelve disciples,
Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya.
21 and, while they were eating, he said, ‘I tell you that one of you will betray me.’
Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”
22 In great grief they began to say to him, one by one, ‘Can it be I, Master?’
Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”
23 ‘The one who dipped his bread beside me in the dish,’ replied Jesus, ‘is the one who will betray me.
Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka.
24 True, the Son of Man must go, as scripture says of him, yet alas for that man by whom the Son of Man is being betrayed! For that man it would be better never to have been born!’
Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
25 Judas, who was betraying him, turned to him and said, ‘Can it be I, Rabbi?’ ‘It is,’ answered Jesus.
Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?” Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”
26 While they were eating, Jesus took some bread, and, after saying the blessing, broke it and, as he gave it to his disciples, said, ‘Take it and eat it; this is my body.’
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
27 Then he took a cup, and, after saying the thanksgiving, gave it to them, with the words, ‘Drink from it, all of you;
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
28 for this is my covenant blood, which is poured out for many for the forgiveness of sins.
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
29 I tell you that I will never, after this, drink of this juice of the grape, until that day when I will drink it new with you in the kingdom of my Father.’
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
30 They then sang a hymn, and went out to the Mount of Olives.
Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.
31 Then Jesus said to them, ‘Even you will all fall away from me tonight. Scripture says – “I will strike down the shepherd, and the sheep of the flock will be scattered.”
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
32 But, after I have risen, I will go before you into Galilee.’
Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
33 ‘If everyone else falls away from you,’ Peter answered, ‘I will never fall away!’
Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”
34 ‘I tell you,’ replied Jesus, ‘that this very night, before the cock crows, you will disown me three times!’
Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”
35 ‘Even if I must die with you,’ Peter exclaimed, ‘I will never disown you!’ All the disciples spoke in the same way.
Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.
36 Then Jesus came with them to a garden called Gethsemane, and he said to his disciples, ‘Sit down here while I go and pray over there.’
Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.”
37 Taking with him Peter and the two sons of Zebedee, he began to show signs of sadness and deep distress of mind.
Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima.
38 ‘I am sad at heart,’ he said, ‘sad even to death; wait here and watch with me.’
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
39 Going on a little further, he threw himself on his face in prayer. ‘My Father,’ he said, ‘if it is possible, let me be spared this cup; only, not as I will, but as you will.’
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
40 Then he came to his disciples, and found them asleep. ‘What!’ he said to Peter, ‘could none of you watch with me for one hour?
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
41 Watch and pray so that you don’t fall into temptation. True, the spirit is eager, but human nature is weak.’
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
42 Again, a second time, he went away, and prayed. ‘My Father,’ he said, ‘if I cannot be spared this cup, but must drink it, your will be done!’
Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”
43 And coming back again he found them asleep, for their eyes were heavy.
Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo.
44 So he left them, and went away again, and prayed a third time, again saying the same words.
Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.
45 Then he came to the disciples, and said, ‘Sleep on now, and rest yourselves. Look – my time is close at hand, and the Son of Man is being betrayed into the hands of wicked people.
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa.
46 Up, and let us be going. Look! My betrayer is close at hand.’
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
47 And, while he was still speaking, Judas, who was one of the Twelve, came in sight; and with him was a great crowd of people, with swords and clubs, sent from the chief priests and elders of the people.
Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu.
48 Now the betrayer had arranged a signal with them. ‘The man whom I kiss,’ he had said, ‘will be the one; arrest him.’
Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.”
49 So he went up to Jesus at once, and exclaimed, ‘Welcome, Rabbi!’ and kissed him;
Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.
50 at which Jesus said to him, ‘Friend, do what you have come for.’ The men went up, seized Jesus, and arrested him.
Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.” Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga.
51 Suddenly one of those who were with Jesus stretched out his hand, and drew his sword, and striking the high priest’s servant, cut off his ear.
Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
52 ‘Sheathe your sword,’ Jesus said, ‘for all who draw the sword will be put to the sword.
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
53 Do you think that I cannot ask my Father for help, when he would at once send to my aid more than twelve legions of angels?
Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri?
54 But in that case how would the scriptures be fulfilled, which say that this must be?’
Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”
55 Jesus at the same time said to the crowds, ‘Have you come out, as if after a robber, with swords and clubs, to take me? I have sat teaching day after day in the Temple Courts, and yet you did not arrest me.’
Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire.
56 The whole of this occurred in fulfilment of the prophetic scriptures. Then the disciples all forsook him and fled.
Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.
57 Those who had arrested Jesus took him to Caiaphas, the high priest, where the teachers of the Law and elders had assembled.
Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana.
58 Peter followed him at a distance as far as the high priest’s courtyard, to see the outcome.
Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.
59 Meanwhile the chief priests and the whole of the High Council were trying to get such false evidence against Jesus, as would warrant putting him to death,
Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.
60 but they did not find any, although many came forward with false evidence. Later on, however, two men came forward and said,
Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka. Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo.
61 ‘This man said “I am able to destroy the Temple of God, and to build it in three days.”’
Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’”
62 Then the high priest stood up, and said to Jesus, ‘Have you no answer? What is this evidence which these men are giving against you?’
Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?”
63 But Jesus remained silent. The high priest said to him, ‘I order you, by the living God, to tell us whether you are the Christ, the Son of God.’
Koma Yesu anakhalabe chete. Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”
64 ‘It is true,’ Jesus answered, ‘Moreover I tell you all that hereafter you will see the Son of Man sitting on the right hand of the Almighty, and coming on the clouds of the heavens.’
Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”
65 Then the high priest tore his robes. ‘This is blasphemy!’ he exclaimed. ‘Why do we want any more witnesses? You have just heard his blasphemy!
Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake.
66 What is your decision?’ They answered, ‘He deserves death.’
Mukuganiza bwanji?” Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”
67 Then they spat in his face, and struck him, while others dealt blows at him, saying as they did so,
Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.
68 ‘Now play the prophet for us, you Christ! Who was it that struck you?’
Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”
69 Peter, meanwhile, was sitting outside in the courtyard; and a maidservant came up to him, and exclaimed, ‘Why, you were with Jesus the Galilean!’
Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”
70 But Peter denied it before them all. ‘I do not know what you mean,’ he replied.
Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”
71 When he had gone out into the gateway, another maid saw him, and said to those who were there, ‘This man was with Jesus of Nazareth!’
Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”
72 Again he denied it with an oath, ‘I do not know the man!’
Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”
73 But soon afterwards those who were standing by came up and said to Peter, ‘You also are certainly one of them; why, even your way of speaking proves it!’
Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”
74 Then Peter said, ‘I swear that I do not know the man! May God punish me if I am lying!’ At that moment a cock crowed;
Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!” Nthawi yomweyo tambala analira.
75 and Peter remembered the words which Jesus had said – “Before a cock has crowed, you will disown me three times”; and he went outside, and wept bitterly.
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.

< Matthew 26 >