< Luke 10 >

1 After this, the Master appointed seventy-two other disciples, and sent them on as his messengers, two and two, in advance, to every town and place that he was himself intending to visit.
Zitatha izi Ambuye anasankha enanso 72 ndi kuwatumiza awiriawiri patsogolo pake ku mzinda uliwonse ndi kumalo kumene Iye anatsala pangʼono kupitako.
2 ‘The harvest,’ he said, ‘is abundant, but the labourers are few. Therefore pray to the owner of the harvest to send labourers to gather in his harvest.
Iye anawawuza kuti, “Zokolola ndi zambiri, koma ogwira ntchito ndi ochepa. Pemphani Ambuye wa zokolola, kuti atumize antchito ku munda wake wa zokolola.
3 Now, go. Remember, I am sending you out as my messengers like lambs among wolves.
Pitani! Ine ndikukutumizani ngati nkhosa pakati pa mimbulu.
4 Do not take a purse with you, or a bag, or sandals; and do not stop to greet anyone on your journey.
Musatenge chikwama kapena thumba kapena nsapato; ndipo musalonjere wina aliyense pa njira.
5 Whatever house you go to stay at, begin by praying for a blessing on it.
“Mukamalowa mʼnyumba, poyamba nenani kuti, ‘Mtendere pa nyumba ino.’
6 Then, if anyone there is deserving of a blessing, your blessing will rest on him; but if not, it will come back on yourselves.
Ngati mʼnyumbamo muli munthu wofuna mtendere, mtendere wanuwo udzakhala pa iyeyo; ngati mulibemo, mtendere wanuwo udzabwerera kwa inu.
7 Remain at that same house, and eat and drink whatever they offer you; for the worker is worth their wages. Do not keep changing from one house to another.
Khalani mʼnyumba yomweyo, idyani ndi kumwa chilichonse chimene akupatsani, pakuti wantchito ayenera kulandira malipiro ake. Musachoke kumene mwafikirako ndi kupita ku nyumba zina.
8 Whatever town you visit, if the people welcome you, eat what is set before you;
“Mukamalowa mʼmudzi, ndi kulandiridwa, idyani chilichonse akukonzerani.
9 cure the sick there, and tell people that the kingdom of God is close at hand.
Chiritsani odwala amene ali kumeneko ndipo muwawuze kuti, ‘Ufumu wa Mulungu wayandikira.’
10 But, whatever town you go to visit, if the people do not welcome you, go out into its streets and say
Koma mukalowa mʼmudzi ndipo osalandiridwa bwino, kapiteni ku misewu mʼmudzimo nʼkukanena kuti,
11 “We wipe off the dust of your town which has clung to Our feet; still, be assured that the kingdom of God is close at Hand.”
‘Tikukusansirani ngakhale fumbi la mʼmudzi wanuwu limene lamamatira ku mapazi athuwa. Komabe dziwani izi: Ufumu wa Mulungu wayandikira.’
12 I tell you that the doom of Sodom will be more bearable on that day than the doom of that town.
Ine ndikuwuzani kuti adzachita chifundo polanga Sodomu pa tsikulo kusiyana ndi mudziwo.
13 Alas for you, Chorazin! Alas for you, Bethsaida! For, if the miracles which have been done in you had been done in Tyre and Sidon, they would have sat in sackcloth and ashes and repented long ago.
“Ndiwe watsoka, iwe Korazini! Ndiwe watsoka, iwe Betisaida! Kukanakhala kuti zodabwitsa zimene zinachitika mwa inu zinachitika ku Turo ndi Sidoni, iwo akanatembenuka mtima kale lomwe, atavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
14 Yet the doom of Tyre and Sidon will be more bearable at the judgment than yours.
Koma adzachita chifundo polanga Turo ndi Sidoni kusiyana ndi inu.
15 And you, Capernaum! Will you exalt yourself to heaven? You will be flung down to Hades. (Hadēs g86)
Kodi iwe Kaperenawo, adzakukweza mpaka kumwamba? Ayi, adzakutsitsa mpaka ku Malo a anthu akufa. (Hadēs g86)
16 Anyone who listens to you is listening to me, and anyone who rejects you is rejecting me; while the person who rejects me is rejecting him who sent me as his messenger.’
“Womvera inu, akumvera Ine; wokana inu, akukana Ine. Ndipo wokana Ine; akukana Iye amene anandituma Ine.”
17 When the seventy-two returned, they exclaimed joyfully, ‘Master, even the demons submit to us when we use your name.’
Anthu 72 aja anabwerera ndi chimwemwe ndipo anati, “Ambuye, ngakhale ziwanda zinatigonjera ife mʼdzina lanu.”
18 And Jesus replied, ‘I have had visions of Satan, fallen, like lightning from the heavens.
Iye anayankha kuti, “Ndinaona Satana akugwa kuchokera kumwamba ngati mphenzi.
19 Remember, I have given you the power to trample on snakes and scorpions, and to meet all the strength of the Enemy. Nothing will ever harm you in any way.
Ine ndakupatsani ulamuliro woponda njoka ndi zinkhanira, ndi kugonjetsa mphamvu zonse za mdani; palibe chimene chidzakupwetekani.
20 Yet do not rejoice in the fact that the spirits submit to you, but rejoice that your names have been enrolled in heaven.’
Komabe musakondwere chifukwa mizimu yoyipa inakugonjerani, koma kondwerani chifukwa mayina anu analembedwa kumwamba.”
21 At that same time, moved to exultation by the Holy Spirit, Jesus said: ‘I thank you, Father, Lord of heaven and earth, that, though you have hidden these things from the wise and learned, you have revealed them to the childlike! Yes, Father, I thank you that this has seemed good to you.
Nthawi imeneyo Mzimu Woyera anadzaza Yesu ndi chimwemwe ndipo anati, “Ine ndikulemekeza Inu, Atate Ambuye a kumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa mwawabisira anthu anzeru ndi ophunzira zinthu izi ndipo mwaziwulula kwa ana aangʼono. Inde, Atate, pakuti munachita zimenezi mwachifuniro chanu.
22 Everything has been committed to me by my Father; nor does anyone know who the Son is, except the Father, or who the Father is, except the Son and those to whom the Son may choose to reveal him.’
“Atate anga anapereka zinthu zonse mʼmanja mwanga. Palibe amene amadziwa Mwana kupatula Atate yekha, ndipo palibe amene amadziwa Atate kupatula Mwana yekha, ndiponso amene Mwanayo akufuna kumuwululira.”
23 Then, turning to his disciples, Jesus said to them alone, ‘Blessed are the eyes that see what you are seeing;
Kenaka anatembenukira kwa ophunzira ake nawawuza iwo okha kuti, “Ndi odala maso amene akuona zimene mukuonazi.
24 for, I tell you, many prophets and kings wished for the sight of the things which you are seeing, yet never heard them.’
Pakuti kunena zoona aneneri ambiri ndi mafumu anafunitsitsa kuona zimene mukuonazi koma sanazione, ndi kumva zimene mukumvazi koma sanazimve.”
25 Just then a student of the Law came forward to test Jesus further. ‘Teacher,’ he said, ‘what must I do if I am to gain eternal life?’ (aiōnios g166)
Nthawi ina katswiri wa malamulo anayimirira kuti ayese Yesu. Iye anati, “Aphunzitsi, ndichite chiyani kuti ndikhale ndi moyo wosatha?” (aiōnios g166)
26 ‘What is said in the Law?’ answered Jesus. ‘What do you read there?’
Yesu anayankha kuti, “Mwalembedwa chiyani mʼMalamulo, ndipo iwe umawerenga zotani?”
27 His reply was – ‘You must love the Lord your God with all your heart, and with all your soul, and with all your strength, and with all your mind; and your neighbour as you love yourself.’
Iye anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse ndi nzeru zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini.”
28 ‘You have answered right,’ said Jesus, ‘Do that, and you will live.’
Yesu anayankha kuti, “Iwe wayankha bwino, chita zimenezi ndipo udzakhala ndi moyo.”
29 But the man, wanting to justify himself, said to Jesus, ‘And who is my neighbour?’
Koma iye anafuna kudzilungamitsa yekha, ndipo anamufunsanso Yesu kuti, “Kodi mnansi wanga ndani?”
30 To which Jesus replied, ‘A man was once going down from Jerusalem to Jericho when he fell into the hands of robbers, who stripped him of everything, and beat him, and went away leaving him half dead.
Yesu pomuyankha anati, “Munthu wina ankatsikira ku Yeriko kuchokera ku Yerusalemu. Pa njira anavulazidwa ndi achifwamba. Anamuvula zovala zake, namumenya ndi kuthawa, namusiya ali pafupi kufa.
31 As it chanced, a priest was going down by that road. He saw the man, but passed by on the opposite side.
Wansembe ankapita pa njira yomweyo, ndipo ataona munthuyo, analambalala.
32 A Levite, too, did the same; he came up to the spot, but, when he saw the man, passed by on the opposite side.
Chimodzimodzinso, Mlevi wina pamene anafika pa malopo ndi kumuona, analambalalanso.
33 But a Samaritan, traveling that way, came upon the man, and, when he saw him, he was moved with compassion.
Koma Msamariya wina, ali pa ulendo wake, anafika pamene panali munthuyo; ndipo atamuona, anamva naye chisoni.
34 He went to him and bound up his wounds, dressing them with oil and wine, and then put him on his own mule, and brought him to an inn, and took care of him.
Anapita panali munthu wovulalayo, nathira mafuta ndi vinyo pa zilonda zake, nʼkuzimanga. Kenaka anamukweza pa bulu wake, napita naye ku nyumba ya alendo, namusamalira.
35 The next day he took out two silver coins and gave them to the innkeeper. “Take care of him,” he said, “and whatever more you may spend I will myself repay you on my way back.”
Mmawa mwake anatenga ndalama ziwiri zasiliva nazipereka kwa woyangʼanira nyumbayo, nati, ‘Musamalireni munthuyu, ndipo pobwera ndidzakubwezerani zonse zimene mugwiritse ntchito.’
36 Now which, do you think, of these three men,’ asked Jesus, ‘proved himself a neighbour to the man who fell into the robbers’ hands?’
“Kodi ukuganiza ndi ndani mwa atatuwa, amene anali mnansi wa munthu amene anavulazidwa ndi achifwambawo?”
37 ‘The one that took pity on him,’ was the answer; at which Jesus said, ‘Go and do the same yourself.’
Katswiri wa Malamulo uja anayankha kuti, “Amene anamuchitira chifundo.” Yesu anamuwuza kuti, “Pita, uzikachita chimodzimodzi.”
38 As they continued their journey, Jesus came to a village, where a woman named Martha welcomed him to her house.
Yesu ndi ophunzira ake akuyenda, anafika pa mudzi kumene mayi wotchedwa Marita anamulandira Iye mʼnyumba mwake.
39 She had a sister called Mary, who seated herself at the Master’s feet, and listened to his teaching;
Mayiyu anali ndi mchemwali wake wotchedwa Mariya, amene anakhala pa mapazi a Yesu kumverera zimene Iye ankanena.
40 but Martha was distracted by the many preparations that she was making. So she went up to Jesus and said, ‘Master, do you approve of my sister’s leaving me to make preparations alone? Tell her to help me.’
Koma Marita anatanganidwa ndi zokonzekera zonse zimene zimayenera kuchitika. Iye anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Ambuye, kodi simusamala kuti mchemwali wanga wandisiya kuti ndichite ntchito yonse ndekha? Muwuzeni andithandize!”
41 ‘Martha, Martha,’ replied the Master, ‘you are anxious and trouble yourself about many things;
Ambuye anati, “Marita, Marita, ukudandaula ndi kuvutika ndi zinthu zambiri,
42 but only a few are necessary, or rather one. Mary has chosen the good part, and it will not be taken away from her.’
koma chofunika nʼchimodzi chokha. Mariya wasankha chinthu chabwino, ndipo palibe angamulande chimenechi.”

< Luke 10 >