< Psalms 37 >

1 Don’t fret because of evildoers, neither be envious against those who work unrighteousness.
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 For they shall soon be cut down like the grass, and wither like the green herb.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Trust in Adonai, and do good. Dwell in the land, and enjoy safe pasture.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Also delight yourself in Adonai, and he will give you the desires of your heart.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Commit your way to Adonai. Trust also in him, and he will do this:
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 he will make your righteousness go out as the light, and your mishpat ·justice· as the noonday sun.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Rest in Adonai, and wait patiently for him. Don’t fret because of him who prospers in his way, because of the man who makes wicked plots happen.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Cease from anger, and forsake wrath. Don’t fret, it leads only to evildoing.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 For evildoers shall be cut off, but those who wait for Adonai shall inherit the land.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 For yet a little while, and the wicked will be no more. Yes, though you look for his place, he is not there.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 But the humble shall inherit the land, and shall delight themselves in the abundance of peace.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 The wicked plots against the just, and gnashes at him with his teeth.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 The Lord will laugh at him, for he sees that his day is coming.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 The wicked have drawn out the sword, and have bent their bow, to cast down the poor and needy, to kill those who are upright on the path.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Their sword shall enter into their own heart. Their bows shall be broken.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Better is a little that the upright has, than the abundance of many wicked.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 For the arms of the wicked shall be broken, but Adonai upholds the upright.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Adonai knows the days of the perfect. Their inheritance shall be forever.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 They shall not be disappointed in the time of evil. In the days of famine they shall be satisfied.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 But the wicked shall perish. The enemies of Adonai shall be like the beauty of the fields. They will vanish— vanish like smoke.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 The wicked borrow, and don’t pay back, but the upright give generously.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 For such as are blessed by him shall inherit the land. Those who are cursed by him shall be cut off.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 A man’s goings are established by Adonai. He delights in his way.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Though he stumble, he shall not fall, for Adonai holds him up with his hand.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 I have been young, and now am old, yet I have not seen the upright forsaken, nor his children begging for bread.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 All day long he deals graciously, and lends. His offspring is blessed.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Depart from evil, and do good. Live securely forever.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 For Adonai 'ahav ·affectionately loves· mishpat ·justice·, and does not forsake his saints. They are preserved forever, but the children of the wicked shall be cut off.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 The upright shall inherit the land, and live in it forever.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 The mouth of the upright talks of wisdom. His tongue speaks mishpat ·justice·.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 The Torah ·Teaching· of his God is in his heart. None of his steps shall slide.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 The wicked watches the upright, and seeks to kill him.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Adonai will not leave him in his hand, nor condemn him when he is judged.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Wait for Adonai, and keep his way, and he will exalt you to inherit the land. When the wicked are cut off, you shall see it.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 I have seen the wicked in great power, spreading himself like a green tree in its native soil.
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 But he passed away, and behold, he was not. Yes, I sought him, but he could not be found.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Mark the perfect man, and see the upright, for there is a future for the man of peace.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 As for transgressors, they shall be destroyed together. The future of the wicked shall be cut off.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 But the salvation of the upright is from Adonai. He is their stronghold in the time of trouble.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Adonai helps them, and rescues them. He rescues them from the wicked, and saves them, Because they have taken refuge in him.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalms 37 >