< Song of Solomon 5 >

1 I have come into my garden, my sister, my bride. I have gathered my myrrh with my spice; I have eaten my honeycomb with my honey; I have drunk my wine with my milk. Eat, friends. Drink, yes, drink abundantly, beloved.
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 I was asleep, but my heart was awake. It is the voice of my beloved who knocks: "Open to me, my sister, my love, my dove, my undefiled; for my head is filled with dew, and my hair with the dampness of the night."
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 I have taken off my robe. Indeed, must I put it on? I have washed my feet. Indeed, must I soil them?
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 My beloved thrust his hand in through the latch opening. My heart pounded for him.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 I rose up to open for my beloved. My hands dripped with myrrh, my fingers with liquid myrrh, on the handles of the lock.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 I opened to my beloved; but my beloved left; and had gone away. My heart went out when he spoke. I looked for him, but I did not find him. I called him, but he did not answer.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 The watchmen who go about the city found me. They beat me. They bruised me. The keepers of the walls took my cloak away from me.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 I adjure you, daughters of Jerusalem, If you find my beloved, that you tell him that I am faint with love.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 How is your beloved better than another beloved, you fairest among women? How is your beloved better than another beloved, that you do so adjure us?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 My beloved is radiant and tan. The best among ten thousand.
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 His head is like the purest gold. His hair is bushy, black as a raven.
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 His eyes are like doves beside the water brooks, washed with milk, mounted like jewels.
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 His cheeks are like a bed of spices with towers of perfumes. His lips are like lilies, dropping liquid myrrh.
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 His hands are like rings of gold set with beryl. His body is like ivory work overlaid with sapphires.
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 His legs are like pillars of marble set on sockets of fine gold. His appearance is like Lebanon, excellent as the cedars.
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 His mouth is sweetness; yes, he is altogether lovely. This is my beloved, and this is my friend, daughters of Jerusalem.
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

< Song of Solomon 5 >