< Psalms 60 >

1 [For the Chief Musician. To the tune of "The Lily of the Covenant." A teaching poem by David, when he fought with Aram Naharaim and with Aram Zobah, and Joab returned, and killed twelve thousand of Edom in the Valley of Salt.] God, you have rejected us. You have broken us down. You have been angry. Restore us, again.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 You have made the land tremble. You have torn it. Mend its fractures, for it quakes.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 You have shown your people hard things. You have made us drink the wine that makes us stagger.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 You have given a banner to those who fear you, that it may be displayed because of the truth. (Selah)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 So that your beloved may be delivered, save with your right hand and answer me.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 God has spoken from his sanctuary: "I will triumph. I will divide Shechem, and measure out the Valley of Succoth.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Gilead is mine, and Manasseh is mine. Ephraim also is the defense of my head. Judah is my scepter.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab is my wash basin. I will throw my shoe on Edom. I shout in triumph over Philistia."
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Who will bring me into the strong city? Who will lead me to Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Haven't you, God, rejected us? You do not go out with our armies, God.
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Give us help against the adversary, for the help of man is vain.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Through God we shall do valiantly, for it is he who will tread down our adversaries.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Psalms 60 >