< Psalms 71 >

1 In you, LORD, I take refuge. Never let me be disappointed.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Deliver me in your righteousness, and rescue me. Turn your ear to me, and save me.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Be to me a rock of refuge to which I may always go. Give the command to save me, for you are my rock and my fortress.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Rescue me, my God, from the hand of the wicked, from the hand of the unrighteous and cruel man.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 For you are my hope, LORD; my confidence from my youth.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 I have relied on you from the womb. From my mother's womb you are my strength. I will always praise you.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 I am a marvel to many, but you are my strong refuge.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 My mouth shall be filled with your praise, with your honor all the day.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Do not reject me in my old age. Do not forsake me when my strength fails.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 For my enemies talk about me. Those who watch for my soul conspire together,
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 saying, "God has forsaken him. Pursue and take him, for no one will rescue him."
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 God, do not be far from me. My God, hurry to help me.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Let my accusers be put to shame and consumed. Let them be covered with disgrace and scorn who want to harm me.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 But I will always hope, and will add to all of your praise.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 My mouth will tell about your righteousness, and of your salvation all day, though I do not know its full measure.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 I will come with the mighty acts of the Lord GOD. I will make mention of your righteousness, even of yours alone.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 God, you have taught me from my youth. Until now, I have declared your wondrous works.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Yes, even when I am old and gray-haired, God, do not forsake me, until I have declared your strength to the next generation, your might to everyone who is to come.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Your righteousness also, God, reaches to the heavens; you have done great things. God, who is like you?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 You, who have shown us many and bitter troubles, you will let me live. You will bring us up again from the depths of the earth.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Increase my honor, and comfort me again.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 I will also praise you with the harp for your faithfulness, my God. I sing praises to you with the lyre, Holy One of Israel.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 My lips shall shout for joy. My soul, which you have redeemed, sings praises to you.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 My tongue will also talk about your righteousness all day long, for they are disappointed, and they are confounded, who want to harm me.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Psalms 71 >