< Psalms 111 >

1 Praise the LORD. I will give thanks to the LORD with my whole heart, in the council of the upright, and in the congregation.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 The LORD's works are great, pondered by all those who delight in them.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 His work is honor and majesty. His righteousness endures forever.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 He has caused his wonderful works to be remembered. The LORD is gracious and merciful.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 He has given food to those who fear him. He always remembers his covenant.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 He has shown his people the power of his works, in giving them the heritage of the nations.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 The works of his hands are truth and justice. All his precepts are sure.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 They are established forever and ever. They are done in truth and uprightness.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 He has sent redemption to his people. He has ordained his covenant forever. His name is holy and awesome.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 The fear of the LORD is the beginning of wisdom. All those who do his work have a good understanding. His praise endures forever.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psalms 111 >