< Lamentations 5 >

1 Remember, LORD, what has come on us. Look, and see our disgrace.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Our inheritance is turned over to strangers, our houses to foreigners.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 We are orphans and fatherless. Our mothers are like widows.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 We have to pay for a drink of water; our wood is sold to us.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Our pursuers are on our necks; we are weary, and have no rest.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 We have submitted to the Egyptians and to the Assyrians, to get enough bread.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Our fathers sinned, and are no more; but we have borne their iniquities.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Servants rule over us: There is none to deliver us out of their hand.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 We get our bread at the peril of our lives, because of the sword in the wilderness.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Our skin is hot like an oven, because of the burning heat of famine.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 They raped the women in Zion, the virgins in the cities of Judah.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Princes were hung by their hands; elders were shown no respect.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 The young men grind at the mill; the boys stagger under loads of wood.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 The elders have gone from the gate, the young men from their music.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 The joy of our heart has ceased; our dancing is turned into mourning.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 The crown is fallen from our head; woe to us, for we have sinned.
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 For this our heart is faint; for these things our eyes grow dim.
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 For the mountain of Zion, which is desolate; the foxes walk on it.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 But you, LORD, abide forever; your throne is from generation to generation.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Why do you keep on forgetting us? Why do you forsake us so long?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Restore us to you, LORD, and we shall be restored; renew our days as in former times,
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 unless you have completely rejected us and are angry with us beyond measure.
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Lamentations 5 >