< Judges 14 >

1 And Samson went down to Timnah, and saw a woman in Timnah of the daughters of the Philistines, and she was right in his eyes.
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
2 He came up, and told his father and his mother, and said, "I have seen a woman in Timnah of the daughters of the Philistines. Now therefore get her for me as wife."
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
3 Then his father and his mother said to him, "Is there not a woman among the daughters of your brothers, or among all my people, that you go to take a wife from the uncircumcised Philistines?" And Samson said to his father, "Get her for me, for she is right in my eyes."
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
4 But his father and his mother did not know that it was of the LORD, for he sought for an opportunity against the Philistines. Now at that time the Philistines had rule over Israel.
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
5 Then Samson went down with his father and his mother to Timnah. And he turned aside and went into the vineyards of Timnah, and look, a young lion roared against him.
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
6 And the Ruach of the LORD rushed upon him, and he tore him as he would have torn a young goat. And he had nothing in his hand, but he did not tell his father or his mother what he had done.
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
7 He went down and talked with the woman, and she was right in Samson's eyes.
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
8 After a while he returned to take her; and he turned aside to see the carcass of the lion, and look, there was a swarm of bees in the body of the lion, and honey.
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
9 He took it into his hands, and went on, eating as he went. And he came to his father and mother, and gave to them, and they ate. But he did not tell them that he had taken the honey out of the body of the lion.
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
10 His father went down to the woman, and Samson made a feast there, since young men used to do so.
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
11 It happened, when they saw him, that they brought thirty companions to be with him.
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
12 Samson said to them, "Let me now put forth a riddle to you. If you can explain it to me within the seven days of the feast, and figure it out, then I will give you thirty linen garments and thirty changes of clothing.
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
13 But if you can't explain it to me, then you shall give me thirty linen garments and thirty changes of clothing." And they said to him, "Propose your riddle, we want to hear it."
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
14 He said to them, "Out of the eater came forth food. Out of the strong came forth sweetness." They couldn't in three days declare the riddle.
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
15 And it happened on the fourth day, that they said to Samson's wife, "Entice your husband, that he may tell us the riddle, lest we burn you and your father's house with fire. Did you invite us here to impoverish us?"
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
16 Samson's wife wept before him, and said, "You just hate me, and do not love me. You have put forth a riddle to the children of my people, and haven't told it me." And he said to her, "Look, I haven't told it to my father or my mother, and shall I tell you?"
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
17 She wept before him the seven days, while their feast lasted: and it happened on the seventh day, that he told her, because she pressed him hard; and she told the riddle to the children of her people.
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
18 The men of the city said to him on the seventh day before the sun went down, "What is sweeter than honey? What is stronger than a lion?" He said to them, "If you hadn't plowed with my heifer, you wouldn't have found out my riddle."
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
19 The Ruach of the LORD rushed upon him, and he went down to Ashkelon, and struck thirty men of them, and took their belongings, and gave their garments to those who explained the riddle. His anger was kindled, and he went up to his father's house.
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
20 But Samson's wife was given to his companion, who had been his friend.
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< Judges 14 >