< Ezekiel 32 >

1 It happened in the twelfth year, in the twelfth month, in the first day of the month, that the word of the LORD came to me, saying,
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 "Son of man, take up a lamentation over Pharaoh king of Egypt, and tell him, 'You were likened to a young lion of the nations: yet you are as a monster in the seas; and you broke out with your rivers, and troubled the waters with your feet, and fouled their rivers.'
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 "Thus says the LORD: 'I will spread out my net on you with a company of many peoples; and they shall bring you up in my net.
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 I will leave you on the land, I will cast you forth on the open field, and will cause all the birds of the sky to settle on you, and I will satisfy the animals of the whole earth with you.
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 I will lay your flesh on the mountains, and fill the valleys with your height.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 I will also water with your blood the land in which you swim, even to the mountains; and the watercourses shall be full of you.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 When I shall extinguish you, I will cover the heavens, and make its stars dark; I will cover the sun with a cloud, and the moon shall not give its light.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 All the bright lights of the sky will I make dark over you, and set darkness on your land, says the LORD.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 I will also trouble the hearts of many peoples, when I shall bring your destruction among the nations, into the countries which you have not known.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Yes, I will make many peoples amazed at you, and their kings shall be horribly afraid for you, when I shall brandish my sword before them; and they shall tremble at every moment, every man for his own life, in the day of your fall.'
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 "For thus says the LORD: 'The sword of the king of Babylon shall come on you.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 By the swords of the mighty will I cause your multitude to fall; the terrible of the nations are they all: and they shall bring to nothing the pride of Egypt, and all its multitude shall be destroyed.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 I will destroy also all its animals from beside many waters; neither shall the foot of man trouble them any more, nor the hoofs of animals trouble them.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Then will I make their waters clear, and cause their rivers to run like oil,' says the LORD.
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 'When I shall make the land of Egypt desolate and waste, a land destitute of that of which it was full, when I shall strike all those who dwell in it, then shall they know that I am the LORD.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 This is the lamentation with which they shall lament; the daughters of the nations shall lament therewith; over Egypt, and over all her multitude, shall they lament therewith,' says the LORD."
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 It happened also in the twelfth year, in the fifteenth day of the month, that the word of the LORD came to me, saying,
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 "Son of man, wail for the multitude of Egypt, and cast them down, even her, and the daughters of the famous nations, to the lower parts of the earth, with those who go down into the pit.
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 'Whom do you pass in beauty? Go down, and be laid with the uncircumcised.'
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 They shall fall in the midst of those who are slain by the sword: she is delivered to the sword; draw her away and all her multitudes.
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 The strong among the mighty shall speak to him out of the midst of Sheol with those who help him: 'They are gone down, they lie still, even the uncircumcised, slain by the sword.' (Sheol h7585)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
22 "Asshur is there and all her company; her graves are all around her; all of them slain, fallen by the sword;
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 whose graves are set in the uttermost parts of the pit, and her company is around her grave; all of them slain, fallen by the sword, who caused terror in the land of the living.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 "There is Elam and all her multitude around her grave; all of them slain, fallen by the sword, who are gone down uncircumcised into the lower parts of the earth, who caused their terror in the land of the living, and have borne their shame with those who go down to the pit.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 They have set her a bed in the midst of the slain with all her multitude; her graves are around her; all of them uncircumcised, slain by the sword; for their terror was caused in the land of the living, and they have borne their shame with those who go down to the pit: he is put in the midst of those who are slain.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 "There is Meshech, Tubal, and all their multitude around her grave; all of them uncircumcised, slain by the sword; for they caused their terror in the land of the living.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 And they are not buried with the fallen warriors of ancient times, who went down to Sheol with their weapons of war, and having their swords placed under their heads, but the punishment for their iniquity rested on their bones; for they were the terror of the mighty in the land of the living. (Sheol h7585)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
28 "But you shall be broken in the midst of the uncircumcised, and shall lie with those who are slain by the sword.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 "There is Edom, her kings and all her princes, who in their might are laid with those who are slain by the sword: they shall lie with the uncircumcised, and with those who go down to the pit.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 "There are the princes of the north, all of them, and all the Sidonians, who are gone down with the slain; in the terror which they caused by their might they are put to shame; and they lie uncircumcised with those who are slain by the sword, and bear their shame with those who go down to the pit.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 "Pharaoh shall see them, and shall be comforted over all his multitude, even Pharaoh and all his army, slain by the sword," says the LORD.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 "For I have put his terror in the land of the living; and he shall be laid in the midst of the uncircumcised, with those who are slain by the sword, even Pharaoh and all his multitude," says the LORD.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 32 >