< Job 34 >

1 Moreover Elihu answered,
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 "Hear my words, you sages. Give ear to me, you who have knowledge.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 For the ear tries words, as the palate tastes food.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Let us choose for us that which is right. Let us know among ourselves what is good.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 For Job has said, 'I am righteous, God has taken away my right:
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Notwithstanding my right I am considered a liar. My wound is incurable, though I am without disobedience.'
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 What man is like Job, who drinks scorn like water,
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Who goes in company with evildoers, and walks with wicked men?
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 For he has said, 'It profits a man nothing that he should delight himself with God.'
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 "Therefore listen to me, you men of understanding: far be it from God, that he should do wickedness, from Shaddai, that he should commit iniquity.
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 For the work of a man he will render to him, and cause every man to find according to his ways.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Yes surely, God will not do wickedly, neither will Shaddai pervert justice.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Who put him in charge of the earth? or who has appointed him over the whole world?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 If he set his heart on himself, If he gathered to himself his spirit and his breath,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 all flesh would perish together, and man would turn again to dust.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 "If now you have understanding, hear this. Listen to the voice of my words.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Shall even one who hates justice govern? Will you condemn him who is righteous and mighty?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Who says to a king, 'Vile.' or to nobles, 'Wicked.'?
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Who doesn't respect the persons of princes, nor regards the rich more than the poor; for they all are the work of his hands.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 In a moment they die, even at midnight. The people are shaken and pass away. The mighty are taken away without a hand.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 "For his eyes are on the ways of a man. He sees all his goings.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 There is no darkness, nor thick gloom, where evildoers may hide themselves.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 For he doesn't need to consider a man further, that he should go before God in judgment.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 He breaks in pieces mighty men in ways past finding out, and sets others in their place.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Therefore he takes knowledge of their works. He overturns them in the night, so that they are destroyed.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 He strikes them as wicked men in the open sight of others;
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 because they turned aside from following him, and wouldn't pay attention to any of his ways,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 so that they caused the cry of the poor to come to him. He heard the cry of the afflicted.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 When he gives quietness, who then can condemn? When he hides his face, who then can see him? Alike whether to a nation, or to a man,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 that the godless man may not reign, that there be no one to ensnare the people.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 "For has any said to God, 'I am guilty, but I will not offend any more.
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Teach me that which I do not see. If I have done iniquity, I will do it no more'?
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Shall his recompense be as you desire, that you refuse it? For you must choose, and not I. Therefore speak what you know.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Men of understanding will tell me, yes, every wise man who hears me:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 'Job speaks without knowledge. His words are without wisdom.'
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 I wish that Job were tried to the end, because of his answering like wicked men.
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 For he adds rebellion to his sin. He claps his hands among us, and multiplies his words against God."
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >