< Isaiah 42 >

1 "Look, my servant I have chosen, my beloved in whom my soul delights. I have put my Spirit on him, and he will bring justice to the nations.
“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
2 He will not shout, nor raise his voice, nor cause it to be heard in the street.
Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
3 He won't break a bruised reed. And he won't extinguish a dimly burning wick. He will faithfully bring justice.
Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
4 He will not grow dim or be crushed, until he has established justice on the earth, and in his name the coastlands will hope."
sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
5 Thus says God, Jehovah, he who created the heavens and stretched them out, he who spread out the earth and that which comes out of it, he who gives breath to its people and spirit to those who walk in it.
Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
6 "I, Jehovah, have called you in righteousness, and will hold your hand, and will keep you, and make you a covenant for the people, as a light for the nations;
“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
7 to open the blind eyes, to bring the prisoners out of the dungeon, and those who sit in darkness out of the prison.
Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
8 "I am Jehovah. That is my name. I will not give my glory to another, nor my praise to engraved images.
“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
9 Look, the former things have happened, and I declare new things. I tell you about them before they come up."
Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
10 Sing to Jehovah a new song, and his praise from the remotest parts of the earth, you who go down to the sea, and all that is in it, the islands and their inhabitants.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Let the desert and its cities cry out, with the villages that Kedar inhabits. Let the inhabitants of Sela sing. Let them shout from the top of the mountains.
Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Let them give glory to Jehovah, and declare his praise in the islands.
Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 Jehovah will go out like a mighty man. He will stir up zeal like a man of war. He will raise a war cry. Yes, he will shout aloud. He will triumph over his enemies.
Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
14 "I have been silent a long time. I have been quiet and restrained myself. Now I will cry out like a travailing woman. I will both gasp and pant.
Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 I will destroy mountains and hills, and dry up all their herbs. I will make the rivers islands, and will dry up the pools.
Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 I will bring the blind by a way that they do not know. I will lead them in paths that they do not know. I will make darkness light before them, and crooked places straight. I will do these things, and I will not forsake them.
Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
17 "Those who trust in engraved images, who tell molten images, 'You are our gods' will be turned back. They will be utterly disappointed.
Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
18 "Hear, you deaf, and look, you blind, that you may see.
“Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
19 Who is blind, but my servant? Or who is as deaf as my messenger whom I send? Who is as blind as he who is at peace, and as blind as Jehovah's servant?
Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 You see many things, but do not observe. His ears are open, but he doesn't listen.
Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 It pleased Jehovah, for his righteousness' sake, to magnify the law, and make it honorable.
Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 But this is a robbed and plundered people. All of them are snared in holes, and they are hidden in prisons. They have become a prey, and no one delivers; and a spoil, and no one says, 'Restore them.'
Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
23 Who is there among you who will give ear to this? Who will listen and hear for the time to come?
Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Who gave Jacob as plunder, and Israel to the robbers? Did not Jehovah, he against whom we have sinned? For they would not walk in his ways, and they disobeyed his law.
Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Therefore he poured the fierceness of his anger on him, and the strength of battle; and it set him on fire all around, but he did not know; and it burned him, but he did not take it to heart."
Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.

< Isaiah 42 >