< Hosea 14 >

1 Israel, return to Jehovah your God; for you have fallen because of your sin.
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Take words with you, and return to Jehovah. Tell him, "Forgive all our sins, and accept that which is good, and we will offer the fruit of our lips.
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Assyria can't save us. We won't ride on horses; neither will we say any more to the work of our hands, 'Our gods.' for in you the fatherless finds mercy."
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 "I will heal their waywardness. I will love them freely; for my anger is turned away from him.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 I will be like the dew to Israel. He will blossom like the lily, and send down his roots like Lebanon.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 His branches will spread, and his beauty will be like the olive tree, and his fragrance like Lebanon.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 They will return and dwell in his shade. They will live and be abundantly satisfied with grain, and blossom like the vine. Their fragrance will be like the wine of Lebanon.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Ephraim, what have I to do any more with idols? I answer, and will take care of him. I am like a green fir tree; from me your fruit is found."
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Who is wise, that he may understand these things? Who is prudent, that he may know them? For the ways of Jehovah are right, and the righteous walk in them; But the rebellious stumble in them.
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.

< Hosea 14 >